Mlaliki 7
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Nzeru
7 Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino,
ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.
2 Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro
kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero:
Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense;
anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.
3 Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka,
pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.
4 Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa,
koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.
5 Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru
kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.
6 Kuseka kwa zitsiru kuli ngati
kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika,
izinso ndi zopandapake.
7 Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru,
ndipo chiphuphu chimawononga mtima.
8 Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake,
ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.
9 Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako,
pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.
10 Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?”
pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.
11 Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino
ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.
12 Nzeru ndi chitetezo,
monganso ndalama zili chitetezo,
koma phindu la chidziwitso ndi ili:
kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.
13 Taganizirani zimene Mulungu wazichita:
ndani angathe kuwongola chinthu
chimene Iye anachipanga chokhota?
14 Pamene zinthu zili bwino, sangalala;
koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino:
Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo,
ndiponso nthawi imene si yabwinoyo.
Choncho munthu sangathe kuzindikira
chilichonse cha mʼtsogolo mwake.
15 Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi:
munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake,
ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.
16 Usakhale wolungama kwambiri
kapena wanzeru kwambiri,
udziwonongerenji wekha?
17 Usakhale woyipa kwambiri,
ndipo usakhale chitsiru,
uferenji nthawi yako isanakwane?
18 Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi,
ndipo usataye njira inayo.
Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.
19 Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru
kupambana olamulira khumi a mu mzinda.
20 Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi
amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.
21 Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula,
mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,
22 pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako
kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.
23 Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati,
“Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,”
koma nzeruyo inanditalikira.
24 Nzeru zimene zilipo,
zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri,
ndani angathe kuzidziwa?
25 Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe,
ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira
ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru
ndiponso kupusa kwake kwa misala.
26 Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa,
mkazi amene ali ngati khoka,
amene mtima wake uli ngati khwekhwe,
ndipo manja ake ali ngati maunyolo.
Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo,
koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.
27 Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi:
“Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,
28 pamene ine ndinali kufufuzabe
koma osapeza kanthu,
ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000,
koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.
29 Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi:
Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama,
koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”
Ecclesiastes 7
New International Version
Wisdom
7 A good name is better than fine perfume,(A)
and the day of death better than the day of birth.(B)
2 It is better to go to a house of mourning
than to go to a house of feasting,
for death(C) is the destiny(D) of everyone;
the living should take this to heart.
3 Frustration is better than laughter,(E)
because a sad face is good for the heart.
4 The heart of the wise is in the house of mourning,
but the heart of fools is in the house of pleasure.(F)
5 It is better to heed the rebuke(G) of a wise person
than to listen to the song of fools.
6 Like the crackling of thorns(H) under the pot,
so is the laughter(I) of fools.
This too is meaningless.
7 Extortion turns a wise person into a fool,
and a bribe(J) corrupts the heart.
8 The end of a matter is better than its beginning,
and patience(K) is better than pride.
9 Do not be quickly provoked(L) in your spirit,
for anger resides in the lap of fools.(M)
10 Do not say, “Why were the old days(N) better than these?”
For it is not wise to ask such questions.
11 Wisdom, like an inheritance, is a good thing(O)
and benefits those who see the sun.(P)
12 Wisdom is a shelter
as money is a shelter,
but the advantage of knowledge is this:
Wisdom preserves those who have it.
13 Consider what God has done:(Q)
Who can straighten
what he has made crooked?(R)
14 When times are good, be happy;
but when times are bad, consider this:
God has made the one
as well as the other.(S)
Therefore, no one can discover
anything about their future.
15 In this meaningless life(T) of mine I have seen both of these:
the righteous perishing in their righteousness,
and the wicked living long in their wickedness.(U)
16 Do not be overrighteous,
neither be overwise—
why destroy yourself?
17 Do not be overwicked,
and do not be a fool—
why die before your time?(V)
18 It is good to grasp the one
and not let go of the other.
Whoever fears God(W) will avoid all extremes.[a]
20 Indeed, there is no one on earth who is righteous,(Z)
no one who does what is right and never sins.(AA)
21 Do not pay attention to every word people say,
or you(AB) may hear your servant cursing you—
22 for you know in your heart
that many times you yourself have cursed others.
23 All this I tested by wisdom and I said,
“I am determined to be wise”(AC)—
but this was beyond me.
24 Whatever exists is far off and most profound—
who can discover it?(AD)
25 So I turned my mind to understand,
to investigate and to search out wisdom and the scheme of things(AE)
and to understand the stupidity of wickedness
and the madness of folly.(AF)
26 I find more bitter than death
the woman who is a snare,(AG)
whose heart is a trap
and whose hands are chains.
The man who pleases God will escape her,
but the sinner she will ensnare.(AH)
27 “Look,” says the Teacher,[b](AI) “this is what I have discovered:
“Adding one thing to another to discover the scheme of things—
28 while I was still searching
but not finding—
I found one upright man among a thousand,
but not one upright woman(AJ) among them all.
29 This only have I found:
God created mankind upright,
but they have gone in search of many schemes.”
Footnotes
- Ecclesiastes 7:18 Or will follow them both
- Ecclesiastes 7:27 Or the leader of the assembly
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.