Mateyu 23
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Yesu Adzudzula Aphunzitsi Amalamulo ndi Afarisi
23 Pamenepo Yesu anati kwa magulu a anthu ndi ophunzira ake: 2 “Aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi amakhala pa mpando wa Mose. 3 Choncho muziwamvera ndi kuchita chilichonse chimene akuwuzani. Koma musachite zimene amachita, popeza sachita zimene amaphunzitsa. 4 Amamanga akatundu olemera nawayika pa mapewa a anthu, koma iwo eni safuna kuwanyamula.
5 “Ntchito zawo amachita ndi cholinga chakuti anthu awaone. Amadzimangirira timaphukusi tikulutikulu ta Mawu a Mulungu pa mphumi ndi pa mkono komanso amatalikitsa mphonje za mikanjo yawo. 6 Amakonda malo aulemu pa maphwando ndi malo ofunika kwambiri mʼmasunagoge. 7 Amakondwera ndi kupatsidwa moni mʼmisika ndi kutchulidwa kuti ‘Aphunzitsi.’
8 “Koma inu simuyenera kutchulidwa ‘Aphunzitsi,’ popeza muli naye Mbuye mmodzi ndipo inu nonse ndinu abale. 9 Ndipo musamatchule wina aliyense pansi pano kuti ‘Atate,’ pakuti muli ndi Atate mmodzi, ndipo ali kumwamba. 10 Komanso musamatchedwenso ‘Mtsogoleri,’ pakuti muli naye Mtsogoleri mmodzi amene ndi Khristu. 11 Wamkulu pakati panu adzakhala wokutumikirani. 12 Pakuti aliyense amene adzikuza adzachepetsedwa, ndipo aliyense amene adzichepetsa adzakuzidwa.
Tsoka kwa Aphunzitsi Amalamulo ndi Afarisi
13 “Tsoka kwa inu aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi achiphamaso! Mumatseka pa khomo la kumwamba kuti anthu asalowemo. Eni akenu simulowamo komanso simulola kuti ena amene akufuna kulowa kuti alowe. 14 Muli ndi tsoka, inu aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, anthu achiphamaso! Mumawadyera akazi amasiye chuma chawo, kwinaku nʼkumanamizira kunena mapemphero ataliatali. Chifukwa cha zimenezi Mulungu adzakulangani koposa.
15 “Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumayenda maulendo ambiri pa mtunda ndi pa nyanja kuti mutembenuze munthu mmodzi, ndipo akatembenuka, mumamusandutsa kukhala mwana wa gehena kawiri kuposa inu.
16 “Tsoka kwa inu, atsogoleri akhungu! Mumati, ‘Ngati wina alumbira kutchula Nyumba ya Mulungu, zilibe kanthu; koma ngati wina alumbira kutchula ndalama zagolide za mʼNyumbayo, wotere ayenera kusunga lumbiro lake.’ 17 Inu akhungu opusa! Chopambana nʼchiyani: ndalama zagolide, kapena Nyumba imene imayeretsa golideyo? 18 Ndiponso mumati, ‘Ngati wina alumbira kutchula guwa lansembe, sizitanthauza kanthu; koma ngati wina alumbira kutchula mphatso ya paguwa lansembe, wotere ayenera kusunga lumbiro lake.’ 19 Inu anthu akhungu! Chopambana nʼchiyani: mphatso, kapena guwa limene limayeretsa mphatsoyo? 20 Chifukwa chake, iye amene alumbira kutchula guwa alumbira pa ilo ndi pa chilichonse chili pamenepo. 21 Ndipo iye wolumbira potchula Nyumba ya Mulungu alumbira pa Nyumbayo ndi pa Iye amene amakhala mʼmenemo. 22 Ndipo iye wolumbira kutchula kumwamba alumbira kutchula mpando waufumu wa Mulungu ndi pa Iye wokhalapo.
23 “Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumapereka chakhumi cha timbewu tonunkhira ndi cha timbewu tokometsera chakudya. Koma mwasiya zofunikira kwambiri za mʼmalamulo monga chilungamo, chifundo ndi kukhulupirika. Muyenera kuchita zomalizirazi komanso osasiya zoyambazo. 24 Atsogoleri akhungu inu! Mumachotsa kantchentche mu chakumwa chanu koma mumameza ngamira.
25 “Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi achiphamaso! Mumayeretsa kunja kwa chikho ndi mbale, koma mʼkatimo mwadzaza ndi dyera ndi kusadziretsa. 26 Afarisi akhungu! Poyamba tsukani mʼkati mwa chikho ndi mbale, ndipo kunja kwake kudzakhalanso koyera.
27 “Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Muli ngati ziliza pa manda zowala kunja zimene zimaoneka zokongola koma mʼkatimo mwadzaza mafupa a anthu akufa ndi zonyansa zina zonse. 28 Chimodzimodzinso, kunja mumaoneka kwa anthu kuti ndinu olungama koma mʼkatimo ndinu odzaza ndi chinyengo ndi zoyipa zina.
29 “Tsoka kwa inu, aphunzitsi amalamulo ndi Afarisi, achiphamaso! Mumamanga ziliza za aneneri ndi kukongoletsa manda a olungama. 30 Ndipo mumati, ‘Ngati tikanakhala mʼmasiku a makolo athu sitikanakhetsa nawo magazi a aneneri.’ 31 Potero mukutsimikiza kuti muli ana a iwo amene anapha aneneri. 32 Dzazani inu muyeso wa uchimo wa makolo anu!
33 “Njoka inu! Ana amamba! Mudzachithawa bwanji chilango cha gehena? 34 Choncho ndi kutumizirani aneneri ndi anthu anzeru ndi aphunzitsi. Ena a iwo mudzawapha ndi kuwapachika; ena mudzawakwapula mʼmasunagoge anu ndi kuwafunafuna kuchokera mudzi wina kufikira wina. 35 Ndipo magazi onse a olungama amene anakhetsedwa pansi pano, kuyambira magazi a Abele, olungama kufikira Zakariya mwana wa Barakiya, amene munamupha pakati pa Nyumba ya Mulungu ndi guwa lansembe, adzakhala pa inu. 36 Zoonadi, ndikuwuzani kuti zonsezi zidzafika pa mʼbado uno.
37 “Haa! Yerusalemu, Yerusalemu, iwe amene umapha aneneri ndi kugenda miyala amene atumidwa kwa iwe, kawirikawiri ndimafuna kusonkhanitsa ana ako, monga nkhuku imasonkhanitsira ana ake pansi pa mapiko ake, koma iwe sunafune. 38 Taona, nyumba yako yasiyidwa ya bwinja. 39 Chifukwa chake ndikuwuza kuti simudzandionanso kufikira pamene mudzati, ‘Wodala Iye amene akudza mʼdzina la Ambuye.’ ”
Matthew 23
Living Bible
23 Then Jesus said to the crowds, and to his disciples, 2 “You would think these Jewish leaders and these Pharisees were Moses, the way they keep making up so many laws![a] 3
5 “Everything they do is done for show. They act holy[b] by wearing on their arms little prayer boxes with Scripture verses inside, and by lengthening the memorial fringes of their robes. 6 And how they love to sit at the head table at banquets and in the reserved pews in the synagogue! 7 How they enjoy the deference paid them on the streets and to be called ‘Rabbi’ and ‘Master’! 8 Don’t ever let anyone call you that. For only God is your Rabbi and all of you are on the same level, as brothers. 9 And don’t address anyone here on earth as ‘Father,’ for only God in heaven should be addressed like that. 10 And don’t be called ‘Master,’ for only one is your master, even the Messiah.
11 “The more lowly your service to others, the greater you are. To be the greatest, be a servant. 12 But those who think themselves great shall be disappointed and humbled; and those who humble themselves shall be exalted.
13-14 “Woe to you, Pharisees, and you other religious leaders. Hypocrites! For you won’t let others enter the Kingdom of Heaven and won’t go in yourselves. And you pretend to be holy, with all your long, public prayers in the streets, while you are evicting widows from their homes. Hypocrites! 15 Yes, woe upon you hypocrites. For you go to all lengths to make one convert, and then turn him into twice the son of hell you are yourselves. 16 Blind guides! Woe upon you! For your rule is that to swear ‘By God’s Temple’ means nothing—you can break that oath, but to swear ‘By the gold in the Temple’ is binding! 17 Blind fools! Which is greater, the gold, or the Temple that sanctifies the gold? 18 And you say that to take an oath ‘By the altar’ can be broken, but to swear ‘By the gifts on the altar’ is binding! 19 Blind! For which is greater, the gift on the altar, or the altar itself that sanctifies the gift? 20 When you swear ‘By the altar,’ you are swearing by it and everything on it, 21 and when you swear ‘By the Temple,’ you are swearing by it and by God who lives in it. 22 And when you swear ‘By heavens,’ you are swearing by the Throne of God and by God himself.
23 “Yes, woe upon you, Pharisees, and you other religious leaders—hypocrites! For you tithe down to the last mint leaf in your garden, but ignore the important things—justice and mercy and faith. Yes, you should tithe, but you shouldn’t leave the more important things undone. 24 Blind guides! You strain out a gnat and swallow a camel.
25 “Woe to you, Pharisees, and you religious leaders—hypocrites! You are so careful to polish the outside of the cup, but the inside is foul with extortion and greed. 26 Blind Pharisees! First cleanse the inside of the cup, and then the whole cup will be clean.
27 “Woe to you, Pharisees, and you religious leaders! You are like beautiful mausoleums—full of dead men’s bones, and of foulness and corruption. 28 You try to look like saintly men, but underneath those pious robes of yours are hearts besmirched with every sort of hypocrisy and sin.
29-30 “Yes, woe to you, Pharisees, and you religious leaders—hypocrites! For you build monuments to the prophets killed by your fathers and lay flowers on the graves of the godly men they destroyed, and say, ‘We certainly would never have acted as our fathers did.’
31 “In saying that, you are accusing yourselves of being the sons of wicked men. 32 And you are following in their steps, filling up the full measure of their evil. 33 Snakes! Sons of vipers! How shall you escape the judgment of hell?
34 “I will send you prophets, and wise men, and inspired writers, and you will kill some by crucifixion, and rip open the backs of others with whips in your synagogues, and hound them from city to city, 35 so that you will become guilty of all the blood of murdered godly men from righteous Abel to Zechariah (son of Barachiah), slain by you in the Temple between the altar and the sanctuary. 36 Yes, all the accumulated judgment of the centuries shall break upon the heads of this very generation.
37 “O Jerusalem, Jerusalem, the city that kills the prophets and stones all those God sends to her! How often I have wanted to gather your children together as a hen gathers her chicks beneath her wings, but you wouldn’t let me. 38 And now your house is left to you, desolate. 39 For I tell you this, you will never see me again until you are ready to welcome the one sent to you from God.”[c]
Footnotes
- Matthew 23:2 keep making up so many laws, literally, “sit on Moses’ seat.”
- Matthew 23:5 act holy, implied. wearing . . . little prayer boxes with Scripture verses inside, literally, “enlarging their phylacteries.”
- Matthew 23:39 from God, literally, “in the name of the Lord.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
The Living Bible copyright © 1971 by Tyndale House Foundation. Used by permission of Tyndale House Publishers Inc., Carol Stream, Illinois 60188. All rights reserved.