Masalimo 3
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Salimo la Davide. Atathawa mwana wake Abisalomu.
3 Inu Yehova, achulukadi adani anga!
Achulukadi amene andiwukira!
2 Ambiri akunena za ine kuti,
“Mulungu sadzamupulumutsa.”
Sela
3 Koma Inu Yehova, ndinu chishango chonditeteza,
Inu mwandiveka ulemerero ndipo mwanditukula.
4 Kwa Yehova, Ine ndilira mofuwula
ndipo Iye amandiyankha kuchokera ku phiri lake loyera.
Sela
5 Ine ndimagona ndi kupeza tulo;
ndimadzukanso chifukwa Yehova amandichirikiza.
6 Sindidzaopa adani anga osawerengeka amene
abwera kulimbana nane kuchokera ku madera onse.
7 Dzukani, Inu Yehova!
Pulumutseni, Inu Mulungu wanga.
Akantheni adani anga onse pa msagwada;
gululani mano a anthu oyipa.
8 Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.
Madalitso akhale pa anthu anu.
Sela
Psalm 3
New International Version
Psalm 3[a]
A psalm of David. When he fled from his son Absalom.(A)
1 Lord, how many are my foes!
How many rise up against me!
2 Many are saying of me,
“God will not deliver him.(B)”[b]
3 But you, Lord, are a shield(C) around me,
my glory, the One who lifts my head high.(D)
4 I call out to the Lord,(E)
and he answers me from his holy mountain.(F)
5 I lie down and sleep;(G)
I wake again,(H) because the Lord sustains me.
6 I will not fear(I) though tens of thousands
assail me on every side.(J)
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.