Masalimo 129
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
129 “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,”
anene tsono Israeli;
2 “Andizunza kwambiri kuyambira ubwana wanga,
koma sanandipambane.
3 Anthu otipula analima pa msana panga
ndipo anapangapo mizere yayitali:
4 Koma Yehova ndi wolungama;
Iye wandimasula ku zingwe za anthu oyipa.”
5 Onse amene amadana ndi Ziyoni
abwezedwe pambuyo mwamanyazi.
6 Akhale ngati udzu womera pa denga la nyumba,
umene umafota usanakule;
7 sungadzaze manja a owumweta
kapena manja a omanga mitolo.
8 Odutsa pafupi asanene kuti,
“Dalitso la Yehova lili pa inu;
tikukudalitsani mʼdzina la Yehova.”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.