Add parallel Print Page Options

20 “Inu Yehova, onani mmene ine ndavutikira!
    Ndikuzunzika mʼkati mwanga,
ndipo mu mtima mwanga ndasautsidwa
    chifukwa ndakhala osamvera.
Mʼmisewu anthu akuphedwa,
    ndipo ku mudzi kuli imfa yokhayokha.

21 “Anthu amva kubuwula kwanga,
    koma palibe wonditonthoza.
Adani anga onse amva masautso anga;
    iwo akusangalala pa zimene Inu mwachita.
Lifikitseni tsiku limene munalonjeza lija
    kuti iwonso adzakhale ngati ine.

22 “Lolani kuti ntchito zawo zoyipa zifike pamaso panu;
    muwalange
ngati mmene mwandilangira ine
    chifukwa cha machimo anga onse.
Ndikubuwula kwambiri
    ndipo mtima wanga walefuka.”

Read full chapter