Add parallel Print Page Options

以色列民錄名於生命冊者必稱聖免難

在那日,七個女人必拉住一個男人,說:「我們吃自己的食物,穿自己的衣服,但求你許我們歸你名下,求你除掉我們的羞恥!」

到那日,耶和華發生的苗必華美尊榮,地的出產必為以色列逃脫的人顯為榮華茂盛。 主以公義的靈和焚燒的靈,將錫安女子的汙穢洗去,又將耶路撒冷中殺人的血除淨。那時,剩在錫安留在耶路撒冷的,就是一切住耶路撒冷在生命冊上記名的,必稱為聖。 耶和華也必在錫安全山並各會眾以上,使白日有煙雲,黑夜有火焰的光,因為在全榮耀之上必有遮蔽。 必有亭子,白日可以得蔭避暑,也可以作為藏身之處,躲避狂風暴雨。

Tsiku limenelo akazi asanu ndi awiri
    adzagwira mwamuna mmodzi,
nʼkunena kuti, “Ife tizidya chakudya chathuchathu,
    ndi kuvala zovala zathu;
inu mungotilola kuti tidziyitanidwa ndi dzina lanu.
    Tichotseni manyazi aumbeta!”

Nthambi ya Yehova

Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli. Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu. Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto. Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova. Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.