Add parallel Print Page Options

17 Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo;
    amaligwadira ndi kulipembedza.
Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti,
    “Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”
18 Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse;
    maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona,
    ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.
19 Palibe amene amayima nʼkulingalira.
    Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti,
chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto;
    pa makala ake ndinaphikira buledi,
    ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya.
Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi.
    Kodi ndidzagwadira mtengo?
20 Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa;
    motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti,
    “Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”

Read full chapter