Add parallel Print Page Options

Ndipo Yehova anati kwa Nowa, “Lowa mu chombo iwe ndi banja lako lonse, chifukwa ndaona kuti ndiwe wolungama mu mʼbado uwu. Pa mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya utengepo zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi zazikazi zisanu ndi ziwirinso. Koma pa mtundu wa nyama iliyonse yosati nʼkudya utengepo zazimuna ziwiri ndi zazikazi ziwirinso. Chimodzimodzinso mbalame, utenge zisanu ndi ziwiri zazimuna ndi zisanu ndi ziwiri zazikazi za mtundu uliwonse kuti mitundu yawo isungike ndi moyo pa dziko lonse lapansi. Pakapita masiku asanu ndi awiri ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku ndipo ndidzawononga cha moyo chilichonse chimene ndinachipanga pa dziko lapansi.”

Ndipo Nowa anachita zonse zimene Yehova anamulamulira.

Pamene chigumula chinabwera pa dziko lapansi Nowa anali ndi zaka 600. Ndipo Nowa, ana ake aamuna, mkazi wake, pamodzi ndi ana ake aakazi analowa mu chombo chija kuthawa madzi a chigumula. Nyama zoti nʼkudya ndi nyama zosadyedwa, mbalame, pamodzi ndi nyama zokwawa zonse zinadza kwa Nowa ziwiriziwiri ndi kulowa mʼchombomo. Ndipo Nowa anatenga ziwiriziwiri, yayimuna ndi yayikazi monga anamulamulira Mulungu. 10 Patapita masiku asanu ndi awiri chigumula chinabwera pa dziko lapansi.

11 Pa tsiku la 17 la mwezi wachiwiri, Nowa ali ndi zaka 600, akasupe onse akuya kwambiri anasefuka ndiponso zitseko za madzi akumwamba zinatsekuka. 12 Ndipo mvula inagwa pa dziko lapansi masiku makumi anayi usana ndi usiku.

13 Linali tsiku lomwelo pamene Nowa ndi ana ake aamuna, Semu, Hamu ndi Yafeti, pamodzi ndi mkazi wake ndi akazi a ana ake atatu aja analowa mu chombo. 14 Iwowa analowa mʼchombomo pamodzi ndi nyama iliyonse ya kutchire monga mwa mtundu wake, ziweto zonse monga mwa mitundu yawo, nyama yokwawa iliyonse monga mwa mtundu wake ndi mbalame iliyonse monga mwa mtundu wake. 15 Nowa analowa mu chombo muja pamodzi ndi zamoyo zonse. 16 Iye analowa nazo zazimuna ndi zazikazi monga mmene Mulungu anamulamulira. Kenaka Yehova anatseka pa khomo.

17 Chigumula chinagwa pa dziko la pansi kwa masiku makumi anayi. Madzi anayamba kuchuluka ndipo ananyamula chombo chija ndi kuchiyandamitsa pamwamba pa dziko. 18 Madzi anafika mwamphamvu ndipo anachulukirachulukira pa dziko lapansi moti chombo chinayandama pamwamba pa madziwo. 19 Madzi a chigumula anabwerabe molimbika motero kuti mapiri ataliatali onse a pa dziko anamizidwa. 20 Madzi anakwera namiza mapiri kwa mamita pafupifupi asanu ndi awiri. 21 Chamoyo chilichonse choyenda pa dziko lapansi chinafa: mbalame, ziweto, nyama zakuthengo, miyandamiyanda ya zonse zolengedwa za pa dziko lapansi pamodzi ndi anthu. 22 Chilichonse chamoyo, chokhala pa mtunda chinafa. 23 Chamoyo chilichonse pa dziko lapansi chinawonongedwa, kuyambira munthu, nyama, zokwawa ndi mbalame. Nowa yekha ndiye anatsala pamodzi ndi onse amene anali naye.

24 Madziwo anadzaza dziko lonse lapansi kwa masiku 150.

The Lord then said to Noah, “Go into the ark, you and your whole family,(A) because I have found you righteous(B) in this generation. Take with you seven pairs of every kind of clean(C) animal, a male and its mate, and one pair of every kind of unclean animal, a male and its mate, and also seven pairs of every kind of bird, male and female, to keep their various kinds alive(D) throughout the earth. Seven days from now I will send rain(E) on the earth(F) for forty days(G) and forty nights,(H) and I will wipe from the face of the earth every living creature I have made.(I)

And Noah did all that the Lord commanded him.(J)

Noah was six hundred years old(K) when the floodwaters came on the earth. And Noah and his sons and his wife and his sons’ wives entered the ark(L) to escape the waters of the flood. Pairs of clean and unclean(M) animals, of birds and of all creatures that move along the ground, male and female, came to Noah and entered the ark, as God had commanded Noah.(N) 10 And after the seven days(O) the floodwaters came on the earth.

11 In the six hundredth year of Noah’s life,(P) on the seventeenth day of the second month(Q)—on that day all the springs of the great deep(R) burst forth, and the floodgates of the heavens(S) were opened. 12 And rain fell on the earth forty days and forty nights.(T)

13 On that very day Noah and his sons,(U) Shem, Ham and Japheth, together with his wife and the wives of his three sons, entered the ark.(V) 14 They had with them every wild animal according to its kind, all livestock according to their kinds, every creature that moves along the ground according to its kind and every bird according to its kind,(W) everything with wings. 15 Pairs of all creatures that have the breath of life in them came to Noah and entered the ark.(X) 16 The animals going in were male and female of every living thing, as God had commanded Noah.(Y) Then the Lord shut him in.

17 For forty days(Z) the flood kept coming on the earth, and as the waters increased they lifted the ark high above the earth. 18 The waters rose and increased greatly on the earth, and the ark floated on the surface of the water. 19 They rose greatly on the earth, and all the high mountains under the entire heavens were covered.(AA) 20 The waters rose and covered the mountains to a depth of more than fifteen cubits.[a][b] (AB) 21 Every living thing that moved on land perished—birds, livestock, wild animals, all the creatures that swarm over the earth, and all mankind.(AC) 22 Everything on dry land that had the breath of life(AD) in its nostrils died. 23 Every living thing on the face of the earth was wiped out; people and animals and the creatures that move along the ground and the birds were wiped from the earth.(AE) Only Noah was left, and those with him in the ark.(AF)

24 The waters flooded the earth for a hundred and fifty days.(AG)

Footnotes

  1. Genesis 7:20 That is, about 23 feet or about 6.8 meters
  2. Genesis 7:20 Or rose more than fifteen cubits, and the mountains were covered