Aroma 8
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Moyo Watsopano mwa Khristu
8 Choncho, tsopano amene ali mwa Khristu Yesu alibe mlandu owatsutsa 2 chifukwa mwa Khristu Yesu, lamulo la Mzimu Woyera amene amapereka moyo, lawamasula ku lamulo la tchimo ndi la imfa. 3 Pakuti zimene Malamulo sanathe kuzichita, popeza anali ofowoka chifukwa cha khalidwe lathu la uchimo, Mulungu anazichita potumiza Mwana wake mʼchifanizo cha munthu ochimwa kuti akhale nsembe yauchimo. Ndipo Iye anagonjetsa tchimo mʼthupi la munthu, 4 ndi cholinga chakuti chilungamo chofunikira cha lamulo chikwaniritsidwe kwathunthu mwa ife amene sitikhala monga mwachikhalidwe chathu cha uchimo koma mwa Mzimu.
5 Pakuti anthu amene amakhala monga mwa makhalidwe oyipa a thupi amayika malingaliro awo pa zinthu zathupi. Koma amene amakhala monga mwa Mzimu amayika malingaliro awo pa zinthu za Mzimu. 6 Kuyika mtima pa zathupi ndi imfa koma kuyika mtima pa za Mzimu ndi moyo ndi mtendere. 7 Pakuti mtima umene wakhazikika pa zathupi ndi wodana ndi Mulungu. Sunagonjere lamulo la Mulungu ndipo sungathe kutero. 8 Ndipo anthu amene amalamulidwa ndi khalidwe lauchimo sangathe kukondweretsa Mulungu.
9 Koma inu simulamulidwanso ndi khalidwe lanu lauchimo koma ndi Mzimu ngati Mzimu wa Mulungu akhaladi mwa inu. Koma ngati munthu aliyense alibe Mzimu wa Khristu, iyeyu si wa Khristu. 10 Ndipo ngati Khristu ali mwa inu, thupi lanu ndi lakufa chifukwa cha uchimo, koma mzimu wanu ndi wamoyo chifukwa cha chilungamo. 11 Ndipo ngati Mzimu wa Mulungu amene anaukitsa Yesu kwa akufa akhala mwa inu, Iyeyo amene anaukitsa Khristu kwa akufa adzapatsanso moyo matupi anu amene amafa kudzera mwa Mzimu wake amene amakhala mwa inu.
12 Kotero abale, ife tili ndi zoti tikwaniritse, koma osati za khalidwe lathu lauchimo, kumachita zofuna zake. 13 Pakuti ngati inu mukhala monga mwa khalidwe lauchimo, mudzafa. Koma ngati mwa Mzimu mupha ntchito zoyipa zathupi, mudzakhala ndi moyo. 14 Onse amene amatsogozedwa ndi Mzimu wa Mulungu ndi ana a Mulungu. 15 Mzimu amene inu munalandira samakusandutsani akapolo, kuti muzikhalanso amantha, koma Mzimu amakusandutsani ana. Ndipo mwa Iye ife timafuwula kuti, “Abba, Atate.” 16 Mzimu mwini amavomerezana ndi mzimu wathu kuti ife ndife ana a Mulungu. 17 Tsono ngati tili ana ake, ndiye kuti ndife olowa mʼmalo a Mulungu ndi olowa mʼmalo pamodzi ndi Khristu. Ngati ife timva zowawa pamodzi ndi Khristu, tidzalandiranso ndi ulemerero womwe pamodzi naye.
Ulemerero wa Mʼtsogolo
18 Ine ndiganiza kuti masautso amene tikuwamva nthawi ino, sakufanana ndi ulemerero umene udzaonetsedwa mwa ife. 19 Pakuti chilengedwe chikudikira ndi chiyembekezo kuonetsedwa poyera kwa ana a Mulungu. 20 Pakuti chilengedwe sichinasankhe kugonjera zopanda pake, koma mwachifuniro cha Iye amene analola kuti chigonjere. Koma chili ndi chiyembekezo 21 chakuti chidzamasulidwa ku ukapolo wa chivundi ndi kulandiranso ufulu ndi ulemerero wa ana a Mulungu.
22 Ife tikudziwa kuti chilengedwe chonse chakhala chikubuwula ndi ululu ngati ululu wa nthawi yobereka mwana mpaka tsopano lino. 23 Si zokhazo ayi, ngakhale ife tomwe, amene tili ndi zipatso zoyamba za Mzimu, tikubuwulira mʼkati mwathu pomwe tikudikira mwachidwi kusankhidwa kwathu ngati ana, kuwomboledwa kwa matupi athu. 24 Pakuti ife tinapulumutsidwa mʼchiyembekezo ichi. Koma chiyembekezo chimene chimaoneka si chiyembekezo ayi. Kodi ndani amene amayembekezera chimene ali nacho kale? 25 Koma ngati ife tiyembekeza chimene tikanalibe, ndiye kuti tikuyembekeza modekha mtima.
26 Momwemonso, Mzimu amatithandiza ife mʼkufowoka kwathu. Ife sitidziwa momwe tiyenera kupempherera koma Mzimu mwini amatipempherera mobuwula ndi mawu osafotokozedwa. 27 Koma Iye amene amasanthula mitima yathu amadziwa maganizo a Mzimu, chifukwa Mzimu amapempherera oyera mtima molingana ndi chifuniro cha Mulungu.
Oposa Agonjetsi
28 Ndipo ife tikudziwa kuti zinthu zonse zimathandizana kuwachitira ubwino amene amakonda Mulungu, amene anayitanidwa monga mwa cholinga chake. 29 Pakuti amene Mulungu anawadziwiratu, anawasankhiratunso kuti akonzedwe mʼchifanizo cha Mwana wake, kuti Iye akhale Mwana woyamba kubadwa mwa abale ambiri. 30 Iwo amene anawasankhiratu, anawayitananso. Amene Iye anawayitana anawalungamitsanso ndipo amene anawalungamitsa anawapatsanso ulemerero.
31 Nanga tsono tidzanena chiyani pa izi? Ngati Mulungu ali mbali yathu, adzatitsutsa ife ndani? 32 Iye amene sanatimane Mwana wake wa Iye yekha, koma anamupereka chifukwa cha ife tonse. Iye adzalekeranjinso pamodzi naye kutipatsa ife zinthu zonse mwaulere? 33 Ndani amene adzabweretsa mlandu kutsutsa amene Mulungu anawasankha? Ndi Mulungu amene amalungamitsa. 34 Ndani amene angatipeze ife olakwa? Palibe. Khristu Yesu amene anafa, kuposera pamenepo, amene anaukitsidwa ndi moyo, amene ali kudzanja lamanja la Mulungu ndiye amene akutipempherera. 35 Ndani amene adzatilekanitsa ife ndi chikondi cha Khristu? Kodi ndi masautso, kapena zowawa, kapena mazunzo, kapena njala, kapena umaliseche, kapena choopsa, kapena lupanga? 36 Monga kwalembedwa:
“Chifukwa cha inu, ife tikuphedwa tsiku lonse:
ife tikutengedwa ngati nkhosa zoti zikaphedwe.”
37 Ayi, mu zonsezi ife ndife oposa agonjetsi mwa Iye amene anatikonda. 38 Pakuti ine ndatsimikiza ndi mtima wonse kuti ngakhale imfa, kapena moyo, ngakhale angelo, kapena ziwanda, ngakhale zinthu zilipo, kapena zili mʼtsogolo, kapena mphamvu zina, 39 ngakhale kutalika, kapena kuya, kapena chilichonse mʼchilengedwe chonse, sizingathe kutisiyanitsa ndi chikondi cha Mulungu chimene chili mwa Khristu Yesu Ambuye athu.
Romans 8
New King James Version
Free from Indwelling Sin
8 There is therefore now no condemnation to those who are in Christ Jesus, (A)who[a] do not walk according to the flesh, but according to the Spirit. 2 For (B)the law of (C)the Spirit of life in Christ Jesus has made me free from (D)the law of sin and death. 3 For (E)what the law could not do in that it was weak through the flesh, (F)God did by sending His own Son in the likeness of sinful flesh, on account of sin: He condemned sin in the flesh, 4 that the righteous requirement of the law might be fulfilled in us who (G)do not walk according to the flesh but according to the Spirit. 5 For (H)those who live according to the flesh set their minds on the things of the flesh, but those who live according to the Spirit, (I)the things of the Spirit. 6 For (J)to be [b]carnally minded is death, but to be spiritually minded is life and peace. 7 Because (K)the [c]carnal mind is enmity against God; for it is not subject to the law of God, (L)nor indeed can be. 8 So then, those who are in the flesh cannot please God.
9 But you are not in the flesh but in the Spirit, if indeed the Spirit of God dwells in you. Now if anyone does not have the Spirit of Christ, he is not His. 10 And if Christ is in you, the body is dead because of sin, but the Spirit is life because of righteousness. 11 But if the Spirit of (M)Him who raised Jesus from the dead dwells in you, (N)He who raised Christ from the dead will also give life to your mortal bodies [d]through His Spirit who dwells in you.
Sonship Through the Spirit
12 (O)Therefore, brethren, we are debtors—not to the flesh, to live according to the flesh. 13 For (P)if you live according to the flesh you will die; but if by the Spirit you (Q)put to death the deeds of the body, you will live. 14 For (R)as many as are led by the Spirit of God, these are sons of God. 15 For (S)you did not receive the spirit of bondage again (T)to fear, but you received the (U)Spirit of adoption by whom we cry out, (V)“Abba,[e] Father.” 16 (W)The Spirit Himself bears witness with our spirit that we are children of God, 17 and if children, then (X)heirs—heirs of God and joint heirs with Christ, (Y)if indeed we suffer with Him, that we may also be glorified together.
From Suffering to Glory
18 For I consider that (Z)the sufferings of this present time are not worthy to be compared with the glory which shall be revealed in us. 19 For (AA)the earnest expectation of the creation eagerly waits for the revealing of the sons of God. 20 For (AB)the creation was subjected to futility, not willingly, but because of Him who subjected it in hope; 21 because the creation itself also will be delivered from the bondage of [f]corruption into the glorious (AC)liberty of the children of God. 22 For we know that the whole creation (AD)groans and labors with birth pangs together until now. 23 Not only that, but we also who have (AE)the firstfruits of the Spirit, (AF)even we ourselves groan (AG)within ourselves, eagerly waiting for the adoption, the (AH)redemption of our body. 24 For we were saved in this hope, but (AI)hope that is seen is not hope; for why does one still hope for what he sees? 25 But if we hope for what we do not see, we eagerly wait for it with perseverance.
26 Likewise the Spirit also helps in our weaknesses. For (AJ)we do not know what we should pray for as we ought, but (AK)the Spirit Himself makes intercession [g]for us with groanings which cannot be uttered. 27 Now (AL)He who searches the hearts knows what the mind of the Spirit is, because He makes intercession for the saints (AM)according to the will of God.
28 And we know that all things work together for good to those who love God, to those (AN)who are the called according to His purpose. 29 For whom (AO)He foreknew, (AP)He also predestined (AQ)to be conformed to the image of His Son, (AR)that He might be the firstborn among many brethren. 30 Moreover whom He predestined, these He also (AS)called; whom He called, these He also (AT)justified; and whom He justified, these He also (AU)glorified.
God’s Everlasting Love
31 What then shall we say to these things? (AV)If God is for us, who can be against us? 32 (AW)He who did not spare His own Son, but (AX)delivered Him up for us all, how shall He not with Him also freely give us all things? 33 Who shall bring a charge against God’s elect? (AY)It is God who justifies. 34 (AZ)Who is he who condemns? It is Christ who died, and furthermore is also risen, (BA)who is even at the right hand of God, (BB)who also makes intercession for us. 35 Who shall separate us from the love of Christ? Shall tribulation, or distress, or persecution, or famine, or nakedness, or peril, or sword? 36 As it is written:
(BC)“For Your sake we are killed all day long;
We are accounted as sheep for the slaughter.”
37 (BD)Yet in all these things we are more than conquerors through Him who loved us. 38 For I am persuaded that neither death nor life, nor angels nor (BE)principalities nor powers, nor things present nor things to come, 39 nor height nor depth, nor any other created thing, shall be able to separate us from the love of God which is in Christ Jesus our Lord.
Footnotes
- Romans 8:1 NU omits the rest of v. 1.
- Romans 8:6 fleshly
- Romans 8:7 fleshly
- Romans 8:11 Or because of
- Romans 8:15 Lit., in Aram., Father
- Romans 8:21 decay
- Romans 8:26 NU omits for us
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Scripture taken from the New King James Version®. Copyright © 1982 by Thomas Nelson. Used by permission. All rights reserved.