Add parallel Print Page Options

Kuweruza Kolungama kwa Mulungu

Choncho, iwe amene umaweruza munthu wina, ulibe pokanira pakuti nthawi iliyonse pamene uweruza wina ukudzitsutsa wekha chifukwa iwe amene umaweruzawe umachitanso zinthu zomwezo. Tsopano ife tikudziwa kuti chiweruzo cha Mulungu, chotsutsa amene amachita zinthu zotere, nʼchokhazikika pa choonadi. Kodi ukuganiza kuti udzathawa chiweruzo cha Mulungu iwe munthu wamba, pamene uweruza ena, iwe ndi kumachitanso zomwezo? Kodi kapena ukupeputsa kukoma mtima kwa Mulungu, kuleza mtima kwake ndi kupirira kwake? Kodi sukuzindikira kuti kukoma mtima kwakeko, nʼkofuna kuti iweyo ulape machimo ako?

Koma pakuti ndiwe wosamvera ndi wa mtima wosafuna kulapa, ukudzisungira chilango pa tsiku la mkwiyo wa Mulungu, pamene chiweruzo cholungama cha Mulungu chidzaonetsedwa. Mulungu adzabwezera aliyense molingana ndi ntchito zake. Iye adzapereka moyo wosatha kwa amene amafunafuna ulemerero, ulemu ndi moyo pochita ntchito zabwino mopirira. Koma Mulungu adzakhuthulira mkwiyo ndi ukali wake pa amene amachita zofuna zawo ndi kukana choonadi nʼkumatsatira zoyipa. Masautso ndi zowawa zidzagwera munthu aliyense amene amachita zonyansa, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina. 10 Koma ulemerero, ulemu ndi mtendere zidzakhala kwa aliyense amene amachita zabwino, kuyambira Myuda kenaka anthu a mitundu ina. 11 Pajatu Mulungu alibe tsankho.

12 Onse amene amachimwa osadziwa Malamulo, adzawonongeka ngakhale kuti sadziwa Malamulowo. Ndipo onse amene amachimwa akudziwa Malamulo adzaweruzidwa potsata Malamulowo. 13 Pakuti si amene amangomva Malamulo amene amakhala wolungama pamaso pa Mulungu, koma ndi okhawo amene amachita zili mʼMalamulomo amene adzatchedwa olungama. 14 Ndithu, pamene a mitundu ina, amene alibe Malamulo, koma mwachikhalidwe chawo amachita zimene zili mʼMalamulo, iwowo ndi Malamulo pa iwo okha, ngakhale kuti alibe Malamulowo. 15 Ntchito zawo zimaonetsa kuti Malamulowo alembedwa mʼmitima mwawo. Chikumbumtima chawonso chimawachitira umboni pakuti maganizo awo amawatsutsa kapena kuwavomereza. 16 Izi zidzachitika pa tsiku limene Mulungu adzaweruza zinsinsi za anthu kudzera mwa Yesu Khristu, monga momwe Uthenga wanga Wabwino unenera.

Ayuda ndi Malamulo

17 Koma iweyo, amene umadzitcha kuti ndiwe Myuda, umadalira Malamulo, ndipo umanyadira ubale wako ndi Mulungu, 18 ngati umadziwa chifuniro chake, ndi kudziwa zoyenera kuchita chifukwa unaphunzitsidwa ndi Malamulo; 19 ngati umadziwadi kuti ndiwe mtsogoleri wa osaona, nyale yowunikira amene ali mu mdima, 20 mlangizi wa anthu opusa, mphunzitsi wa makanda, chifukwa umadziwa kuti mʼMalamulo uli nayo nzeru yonse ndi choonadi, 21 tsono, iwe amene umaphunzitsa ena, sudziphunzitsa wekha kodi? Kodi iwe amene umalalikira kuti anthu asabe, umabanso? 22 Kodi iwe amene umanena kuti anthu asachite chigololo, umachitanso chigololo? Kodi iwe amene umanyasidwa ndi mafano, umalandanso za mʼnyumba zopembedzera mafanowo? 23 Kodi iwe amene umadzitama ndi Malamulo, umamuchititsa manyazi Mulungu posamvera Malamulowo? 24 Monga kwalembedwa, “Dzina la Mulungu likuchitidwa chipongwe pakati pa a mitundu ina chifukwa cha inu.”

25 Mdulidwe umakhala ndi phindu ngati usunga Malamulo, koma ngati sumvera Malamulo, iweyo umakhala ngati kuti sunachite mdulidwe. 26 Ngati amene sanachite mdulidwe achita zomwe zili mʼMalamulo, kodi sadzatengedwa ngati ochita mdulidwe? 27 Munthu amene sanachite mdulidwe mʼthupi koma amamvera Malamulo adzakutsutsa iwe wosamvera Malamulowe, ngakhale kuti uli nawo Malamulo olembedwawo.

28 Myuda weniweni si amene angooneka ngati Myuda pamaso pa anthu, ndipo mdulidwe weniweni si umene umangochitika mʼthupi pamaso pa anthu. 29 Ayi, Myuda weniweni ndi amene ali Myuda mu mtima mwake, ndipo mdulidwe weniweni ndi wa mtima, wochitika ndi Mzimu, osati ndi malamulo olembedwa. Woyamikira munthu wotere ndi Mulungu, osati anthu ayi.

God’s Righteous Judgment

Therefore you are (A)inexcusable, O man, whoever you are who judge, (B)for in whatever you judge another you condemn yourself; for you who judge practice the same things. But we know that the judgment of God is according to truth against those who practice such things. And do you think this, O man, you who judge those practicing such things, and doing the same, that you will escape the judgment of God? Or do you despise (C)the riches of His goodness, (D)forbearance, and (E)longsuffering, (F)not knowing that the goodness of God leads you to repentance? But in accordance with your hardness and your [a]impenitent heart (G)you are [b]treasuring up for yourself wrath in the day of wrath and revelation of the righteous judgment of God, who (H)“will render to each one according to his deeds”: eternal life to those who by patient continuance in doing good seek for glory, honor, and immortality; but to those who are self-seeking and (I)do not obey the truth, but obey unrighteousness—indignation and wrath, tribulation and anguish, on every soul of man who does evil, of the Jew (J)first and also of the [c]Greek; 10 (K)but glory, honor, and peace to everyone who works what is good, to the Jew first and also to the Greek. 11 For (L)there is no partiality with God.

12 For as many as have sinned without law will also perish without law, and as many as have sinned in the law will be judged by the law 13 (for (M)not the hearers of the law are just in the sight of God, but the doers of the law will be justified; 14 for when Gentiles, who do not have the law, by nature do the things in the law, these, although not having the law, are a law to themselves, 15 who show the (N)work of the law written in their hearts, their (O)conscience also bearing witness, and between themselves their thoughts accusing or else excusing them) 16 (P)in the day when God will judge the secrets of men (Q)by Jesus Christ, (R)according to my gospel.

The Jews Guilty as the Gentiles

17 [d]Indeed (S)you are called a Jew, and (T)rest[e] on the law, (U)and make your boast in God, 18 and (V)know His will, and (W)approve the things that are excellent, being instructed out of the law, 19 and (X)are confident that you yourself are a guide to the blind, a light to those who are in darkness, 20 an instructor of the foolish, a teacher of babes, (Y)having the form of knowledge and truth in the law. 21 (Z)You, therefore, who teach another, do you not teach yourself? You who preach that a man should not steal, do you steal? 22 You who say, “Do not commit adultery,” do you commit adultery? You who abhor idols, (AA)do you rob temples? 23 You who (AB)make your boast in the law, do you dishonor God through breaking the law? 24 For (AC)“the name of God is (AD)blasphemed among the Gentiles because of you,” as it is written.

Circumcision of No Avail

25 (AE)For circumcision is indeed profitable if you keep the law; but if you are a breaker of the law, your circumcision has become uncircumcision. 26 Therefore, (AF)if an uncircumcised man keeps the righteous requirements of the law, will not his uncircumcision be counted as circumcision? 27 And will not the physically uncircumcised, if he fulfills the law, (AG)judge you who, even with your [f]written code and circumcision, are a transgressor of the law? 28 For (AH)he is not a Jew who is one outwardly, nor is circumcision that which is outward in the flesh; 29 but he is a Jew (AI)who is one inwardly; and (AJ)circumcision is that of the heart, (AK)in the Spirit, not in the letter; (AL)whose [g]praise is not from men but from God.

Footnotes

  1. Romans 2:5 unrepentant
  2. Romans 2:5 storing
  3. Romans 2:9 Gentile
  4. Romans 2:17 NU But if
  5. Romans 2:17 rely
  6. Romans 2:27 Lit. letter
  7. Romans 2:29 A play on words—Jew is literally praise.