Ahebri 1
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Khristu Mwana wa Mulungu Aposa Angelo
1 Kale lija Mulungu ankayankhula ndi makolo athu pa nthawi zosiyanasiyana ndiponso mwa njira zosiyanasiyana kudzera mwa aneneri. 2 Koma masiku otsiriza ano, Mulungu wayankhula nafe kudzera mwa Mwana wake. Mwanayu anamusankha kuti akhale mwini wa zinthu zonse, ndiponso Mulungu analenga dziko lonse kudzera mwa Iye. 3 Mwanayo ndiye kuwala kwa ulemerero wa Mulungu, chithunzithunzi chenicheni cha khalidwe lake. Iyeyu amachirikiza zinthu zonse ndi mphamvu ya mawu ake. Iye atayeretsa anthu kuchoka ku machimo awo, anakhala pansi kumwamba kudzanja lamanja la Mulungu waulemerero. 4 Mwanayu ndi wamkulu koposa angelo, monga momwe dzina limene analandira limaposa dzina la angelo.
5 Kodi ndi kwa mngelo uti, kumene Mulungu anati,
“Iwe ndiwe mwana wanga;
Ine lero ndakhala Atate ako.”
Kapena kunenanso kuti,
“Ine ndidzakhala abambo ake;
iye adzakhala mwana wanga.”
6 Pamene Mulungu amatuma Mwana wake woyamba kubadwa ku dziko lapansi anati,
“Angelo onse a Mulungu amupembedze Iye.”
7 Iye ponena za angelo akuti,
“Mulungu amasandutsa angelo ake mphepo,
amasandutsa atumiki ake malawi amoto.”
8 Koma za Mwana wake akuti,
“Inu Mulungu, mpando wanu waufumu udzakhala mpaka muyaya,
ndipo mudzaweruza molungama mu ufumu wanu.
9 Mwakonda chilungamo ndi kudana ndi zoyipa;
Nʼchifukwa chake, Mulungu wanu wakukwezani kuposa anzanu
pokudzozani mafuta osonyeza chimwemwe.”
10 Mulungu akutinso,
“Ambuye, pachiyambi Inu munayika maziko a dziko lapansi;
ndipo zakumwambako ndi ntchito za manja anu.
11 Zimenezi zidzatha, koma Inu ndinu wachikhalire.
Izo zidzatha ngati zovala.
12 Mudzazipindapinda ngati chofunda;
ndipo zidzasinthidwa ngati chovala.
Koma Inu simudzasintha,
ndipo zaka zanu sizidzatha.”
13 Kodi ndi kwa Mngelo uti kumene Mulungu ananenapo kuti,
“Khala kudzanja langa lamanja
mpaka nditapanga adani ako
kukhale chopondapo mapazi ako.”
14 Kodi angelo onse si mizimu yotumikira odzalandira chipulumutso?
Hebrews 1
New International Version
God’s Final Word: His Son
1 In the past God spoke(A) to our ancestors through the prophets(B) at many times and in various ways,(C) 2 but in these last days(D) he has spoken to us by his Son,(E) whom he appointed heir(F) of all things, and through whom(G) also he made the universe.(H) 3 The Son is the radiance of God’s glory(I) and the exact representation of his being,(J) sustaining all things(K) by his powerful word. After he had provided purification for sins,(L) he sat down at the right hand of the Majesty in heaven.(M) 4 So he became as much superior to the angels as the name he has inherited is superior to theirs.(N)
The Son Superior to Angels
5 For to which of the angels did God ever say,
Or again,
6 And again, when God brings his firstborn(Q) into the world,(R) he says,
7 In speaking of the angels he says,
8 But about the Son he says,
“Your throne, O God, will last for ever and ever;(U)
a scepter of justice will be the scepter of your kingdom.
9 You have loved righteousness and hated wickedness;
therefore God, your God, has set you above your companions(V)
by anointing you with the oil(W) of joy.”[e](X)
10 He also says,
“In the beginning, Lord, you laid the foundations of the earth,
and the heavens are the work of your hands.(Y)
11 They will perish, but you remain;
they will all wear out like a garment.(Z)
12 You will roll them up like a robe;
like a garment they will be changed.
But you remain the same,(AA)
and your years will never end.”[f](AB)
13 To which of the angels did God ever say,
14 Are not all angels ministering spirits(AF) sent to serve those who will inherit(AG) salvation?(AH)
Footnotes
- Hebrews 1:5 Psalm 2:7
- Hebrews 1:5 2 Samuel 7:14; 1 Chron. 17:13
- Hebrews 1:6 Deut. 32:43 (see Dead Sea Scrolls and Septuagint)
- Hebrews 1:7 Psalm 104:4
- Hebrews 1:9 Psalm 45:6,7
- Hebrews 1:12 Psalm 102:25-27
- Hebrews 1:13 Psalm 110:1
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.