Add parallel Print Page Options

Ana a Israeli

Ana a Israeli anali awa:

Rubeni, Simeoni, Levi, Yuda, Isakara, Zebuloni, Dani, Yosefe, Benjamini, Nafutali, Gadi ndi Aseri.

Yuda Mpaka pa Ana a Hezironi

Ana a Hezironi

Ana a Yuda anali awa:

Eri, Onani ndi Sela. Ana atatu awa anabereka ndi mkazi wa Chikanaani, Batisuwa. Eri, mwana woyamba wa Yuda anali woyipa kwambiri pamaso pa Yehova, kotero Yehova anamupha. Mpongozi wake Tamara anamuberekera Perezi ndi Zera. Ana onse a Yuda analipo asanu.

Ana a Perezi anali awa:

Hezironi ndi Hamuli.

Ana a Zera anali awa:

Zimuri, Etani, Hemani, Kalikoli ndi Dara. Onse analipo asanu.

Mwana wa Karimi anali

Akani, amene anabweretsa mavuto pakati pa Israeli pamene anatenga zinthu zoyenera kuwonongedwa.

Mwana wa Etani anali

Azariya.

Ana amene anabadwa kwa Hezironi anali:

Yerahimeeli, Ramu ndi Kelubai.

Kuchokera kwa Ramu Mwana wa Hezironi

10 Ramu anabereka

Aminadabu ndipo Aminadabu anali abambo ake a Naasoni, mtsogoleri wa fuko la Yuda. 11 Naasoni anabereka Salima, Salima anabereka Bowazi, 12 Bowazi anabereka Obedi ndipo Obedi anabereka Yese.

13 Yese anabereka

Eliabu mwana wake woyamba, wachiwiri Abinadabu, wachitatu Simea, 14 wachinayi Netaneli, wachisanu Radai, 15 wachisanu ndi chimodzi Ozemu ndi wachisanu ndi chiwiri Davide. 16 Alongo awo anali Zeruya ndi Abigayeli. Ana atatu a Zeruya anali Abisai Yowabu ndi Asaheli. 17 Abigayeli anali amayi ake a Amasa amene abambo ake anali Yeteri wa fuko la Ismaeli.

Kalebe Mwana wa Hezironi

18 Kalebe mwana wa Hezironi anabereka ana mwa Azuba mkazi wake (ndi mwa Yerioti). Ana a mkaziyo anali awa: Yeseri, Sobabu ndi Aridoni. 19 Azuba atamwalira, Kalebe anakwatira Efurata, amene anamuberekera Huri. 20 Huri anabereka Uri ndipo Uri anabereka Bezaleli.

21 Patapita nthawi, Hezironi anagona ndi mwana wamkazi wa Makiri abambo ake a Giliyadi (iye anamukwatira ali ndi zaka 60) ndipo anamuberekera Segubu. 22 Segubu anabereka Yairi, amene anali ndi mizinda 23 ku Giliyadi. 23 (Koma Gesuri ndi Aramu analanda Havoti Yairi komanso Kenati ndi madera ake onse ozungulira, mizinda makumi asanu ndi umodzi). Onsewa anali adzukulu, a Makiri abambo ake a Giliyadi.

24 Atamwalira Hezironi ku Kalebe Efurata, Abiya mkazi wa Hezironi anamuberekera Asihuri abambo a Tekowa.

Yerahimeeli Mwana wa Hezironi

25 Ana a Yerahimeeli, mwana woyamba wa Hezironi anali:

Ramu, mwana wake woyamba, Buna, Oreni, Ozemu ndi Ahiya. 26 Yerahimeeli anali ndi mkazi wina amene dzina lake linali Atara, amene anali amayi a Onamu.

27 Ana a Ramu, mwana woyamba wa Yerahimeeli, anali awa:

Maazi, Yamini ndi Ekeri.

28 Ana a Onamu anali awa:

Shamai ndi Yada.

Ana a Shamai anali awa:

Nadabu ndi Abisuri.

29 Mkazi wa Abisuri anali Abihaili, amene anamuberekera Ahibani ndi Molidi.

30 Ana a Nadabu anali awa:

Seledi ndi Apaimu. Koma Seledi anamwalira wopanda ana.

31 Ana a Apaimu anali awa:

Isi, amene anabereka Sesani.

Sesani anabereka Ahilai.

32 Ana a Yada, mʼbale wa Samai, anali awa:

Yereri ndi Yonatani. Koma Yeteri anamwalira wopanda ana.

33 Ana a Yonatani anali awa:

Peleti ndi Zaza.

Amenewa anali adzukulu a Yerahimeeli.

34 Sesani sanabereke ana aamuna koma aakazi okhaokha.

Iye anali ndi wantchito wa ku Igupto, dzina lake Yariha. 35 Sesani anapereka mwana wake wamkazi kwa Yariha wantchito wake kuti amukwatire ndipo anamuberekera Atayi.

36 Atayi anali abambo ake a Natani,

Natani anali abambo ake a Zabadi,

37 Zabadi anali abambo a Efilali,

Efilali anali abambo a Obedi,

38 Obedi anali abambo a Yehu,

Yehu anali abambo a Azariya,

39 Azariya anali abambo a Helezi,

Helezi anali abambo a Eleasa,

40 Eleasa anali abambo ake a Sisimai,

Sisimai anali abambo a Salumu,

41 Salumu anali abambo a Yekamiya,

Yekamiya anali abambo a Elisama.

Mabanja a Kalebe

42 Ana a Kalebe mʼbale wa Yerahimeeli anali awa:

Mesa mwana wachisamba, anali abambo a Zifi, ndipo mwana wake Maresa anali abambo a Hebroni.

43 Ana a Hebroni anali awa:

Kora, Tapuwa, Rekemu ndi Sema. 44 Sema anali abambo ake Rahamu ndipo Rahamu anali abambo a Yorikeamu. Rekemu anali abambo a Samai. 45 Mwana wa Samai anali Maoni, ndipo Maoni anali abambo a Beti Zuri.

46 Efai, mzikazi wa Kalebe, anali amayi a Harani, Moza ndi Gazezi. Harani anali abambo a Gazezi.

47 Ana a Yahidai anali awa:

Regemu, Yotamu, Gesani, Peleti, Efai ndi Saafi.

48 Maaka mzikazi wa Kalebe anali mayi Seberi ndi Tirihana. 49 Iye anaberekanso Saafi abambo a Madimena ndi Seva abambo a Makibena ndi Gibeya. Mwana wamkazi wa Kalebe anali Akisa. 50 Izi zinali zidzukulu za Kalebe.

Ana a Huri mwana wachisamba wa Efurata anali awa:

Sobala abambo a Kiriati Yearimu, 51 Salima abambo a Betelehemu ndi Harefu abambo ake a Beti-Gadera.

52 Zidzukulu za Sobala abambo a Kiriati Yearimu zinali izi:

Harowe, theka la banja la Manahati, 53 ndipo mabanja a Kiriati-Yeyarimu anali awa: Aitiri, Aputi, Asumati ndi Amisirai. Azorati ndi Aesitaoli anachokera kwa amenewa.

54 Zidzukulu za Salima zinali izi:

Betelehemu, Anetofati, Atiroti-Beti-Yowabu, theka la banja la Manahati, Azori, 55 ndiponso mabanja a alembi amene amakhala ku Yabesi: Atiroti, Asimeati ndiponso Asukati. Awa ndi Akeni amene anachokera kwa Hamati, kholo la Arekabu.

以色列的后裔

以色列的儿子是吕便、西缅、利未、犹大、以萨迦、西布伦、 但、约瑟、便雅悯、拿弗他利、迦得、亚设。

犹大的后裔

犹大的儿子是珥、俄南和示拉。这三人是迦南人书亚的女儿生的。犹大的长子珥在耶和华眼中是个邪恶的人,因而被耶和华击杀了。 犹大的儿媳她玛给犹大生了法勒斯和谢拉。犹大共有五个儿子。 法勒斯的儿子是希斯仑和哈姆勒。 谢拉的五个儿子是心利、以探、希幔、甲各、大拉。 迦米的儿子是亚干,这亚干私藏本该毁灭的东西,连累了以色列人。 以探的儿子是亚撒利雅。

希斯仑的儿子是耶拉篾、兰和迦勒[a] 10 兰生亚米拿达,亚米拿达生拿顺,拿顺是犹大人的首领。 11 拿顺生撒门,撒门生波阿斯, 12 波阿斯生俄备得,俄备得生耶西。 13 耶西生长子以利押、次子亚比拿达、三子示米亚、 14 四子拿坦业、五子拉代、 15 六子阿鲜、七子大卫。 16 他们的姊妹是洗鲁雅和亚比该。洗鲁雅的三个儿子是亚比筛、约押和亚撒黑。 17 亚比该生亚玛撒,亚玛撒的父亲是以实玛利人益帖。

希斯仑的后裔

18 希斯仑的儿子迦勒和妻子阿苏巴生了儿子,他也和耶略生了儿子。阿苏巴的儿子是耶设、朔罢和押墩。 19 阿苏巴死后,迦勒又娶了以法她,生了户珥。 20 户珥生乌利,乌利生比撒列。 21 希斯仑六十岁娶玛吉的女儿,与她生了西割。玛吉是基列的父亲。 22 西割生雅珥,雅珥在基列有二十三座城邑。 23 后来基述人和亚兰人夺取了雅珥的城邑,包括基纳及其附近的六十个村落。这些人都是基列的父亲玛吉的后代。 24 希斯仑死在迦勒·以法他后,他的妻子亚比雅给他生了亚施户。亚施户是提哥亚的父亲。

耶拉篾的后裔

25 希斯仑的长子耶拉篾生了长子兰,又生了布拿、阿连、阿鲜、亚希雅。 26 耶拉篾的另一个妻子名叫亚他拉,是阿南的母亲。 27 耶拉篾的长子兰的儿子是玛斯、雅悯和以结。 28 阿南的儿子是沙迈和雅大。沙迈的儿子是拿答和亚比述。 29 亚比述的妻子名叫亚比孩,他们生了亚班和摩利。 30 拿答的儿子是西列和亚遍。西列死后没有留下儿子。 31 亚遍的儿子是以示,以示的儿子是示珊,示珊的儿子是亚来。 32 沙迈的兄弟雅大的儿子是益帖和约拿单。益帖死后没有留下儿子。 33 约拿单的儿子是比勒和撒萨。这些人都是耶拉篾的子孙。 34 示珊没有儿子,只有女儿,还有一个名叫耶哈的埃及仆人。 35 示珊把女儿嫁给仆人耶哈,他们生了亚太。 36 亚太生拿单,拿单生撒拔, 37 撒拔生以弗拉,以弗拉生俄备得, 38 俄备得生耶户,耶户生亚撒利雅, 39 亚撒利雅生希利斯,希利斯生以利亚萨, 40 以利亚萨生西斯迈,西斯迈生沙龙, 41 沙龙生耶加米雅,耶加米雅生以利沙玛。

迦勒的后裔

42 耶拉篾的兄弟迦勒的长子是西弗的父亲米沙,希伯仑的父亲玛利沙也是迦勒的儿子。 43 希伯仑的儿子是可拉、他普亚、利肯、示玛。 44 示玛生拉含,拉含是约干的父亲。利肯生沙迈, 45 沙迈的儿子是玛云,玛云是伯·夙的父亲。 46 迦勒的妾以法生哈兰、摩撒和迦谢。哈兰生迦谐。 47 雅代的儿子是利健、约坦、基珊、毗力、以法、沙亚弗。 48 迦勒的妾玛迦生示别、特哈拿、 49 麦玛拿的父亲沙亚弗、抹比拿和基比亚的父亲示法。迦勒的女儿是押撒。 50 这些人都是迦勒的子孙。 以法她的长子户珥生基列·耶琳的父亲朔巴、 51 伯利恒的父亲萨玛、伯迦得的父亲哈勒。 52 基列·耶琳的父亲朔巴的子孙是哈罗以和半数米努·哈人。 53 基列·耶琳的各宗族是以帖人、布特人、舒玛人、密来人,从这些宗族中又衍生出琐拉人和以实陶人。 54 萨玛的后代是伯利恒人、尼陀法人、亚他绿·伯·约押人、半数玛拿哈人、琐利人, 55 以及住在雅比斯的文书世家特拉人、示米押人和苏甲人。这些都是基尼人,是利甲家族的祖先哈末的后代。

Footnotes

  1. 2:9 迦勒”希伯来文是“基路拜”,“迦勒”的另一种拼法。