1 Mbiri 10
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Sauli Adzipha Yekha
10 Tsono Afilisti anachitanso nkhondo ndi Aisraeli ndipo Aisraeli anathawa Afilistiwo, kotero kuti ambiri anaphedwa pa phiri la Gilibowa. 2 Afilisti anapanikiza kwambiri Sauli ndi ana ake, ndipo anapha Yonatani, Abinadabu ndi Maliki-Suwa. 3 Nkhondo inakula kwambiri mozungulira Sauli ndipo pamene anthu amauta anamupeza, anamuvulaza.
4 Tsono Sauli anawuza mnyamata wake wonyamula zida zake kuti, “Solola lupanga lako undiphe, kuopa kuti anthu osachita mdulidwewa angabwere ndi kudzandizunza ine.”
Koma mnyamata wonyamula zida uja anachita mantha kwambiri ndipo sanathe kutero. Choncho Sauli anatenga lupanga lake lomwe nagwerapo. 5 Mnyamata wonyamula zida zake uja ataona kuti Sauli wafa, nayenso anadzigwetsera pa lupanga lake nafa. 6 Motero Sauli ndi ana ake atatu anafa, pamodzi ndi banja lake lonse anafera limodzi.
7 Pamene Aisraeli onse amene anali mʼchigwa anaona kuti gulu lankhondo lathawa komanso kuti Sauli ndi ana ake aphedwa, nawonso anathawa kusiya mizinda yawo. Ndipo Afilisti anabwera kudzakhalamo.
8 Mmawa mwake, Afilisti atabwera kudzatenga zinthu za anthu ophedwa, anapeza Sauli ndi ana ake atafa pa phiri la Gilibowa. 9 Iwo anamuvula zovala zake, natenga mutu wake ndi zida zake zankhondo. Ndipo anatumiza amithenga mʼdziko lonse la Afilisti kukafalitsa nkhani yabwinoyi kwa mafano awo ndi kwa anthu awo. 10 Iwo anayika zida zake zankhondo mʼnyumba zopembedzera milungu yawo ndipo anapachika mutu wake mʼnyumba ya Dagoni.
11 Pamene anthu onse okhala ku Yabesi Giliyadi anamva zimene Afilisti anachitira Sauli, 12 anthu awo onse olimba mtima anapita kukatenga mitembo ya Sauli ndi ana ake ndipo anabwera nayo ku Yabesi. Anakwirira mafupa awo pansi pa mtengo wabwemba ku Yabesi, ndipo anasala kudya masiku asanu ndi awiri.
13 Sauli anafa chifukwa anali wosakhulupirika pamaso pa Yehova. Iye sanasunge mawu a Yehova, pakuti anakafunsira nzeru kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, 14 sanafunsire nzeruzo kwa Yehova. Choncho Yehova anamupha ndi kupereka ufumu kwa Davide mwana wa Yese.
历代志上 10
Chinese Contemporary Bible (Simplified)
扫罗之死
10 非利士人与以色列人交战,以色列人败逃,许多人在基利波山被杀。 2 非利士人穷追扫罗及其众子,杀了扫罗的儿子约拿单、亚比拿达和麦基舒亚。 3 扫罗周围的战斗非常猛烈,他被弓箭手发现、射成重伤, 4 就对为他拿兵器的人说:“拔出你的刀来刺死我吧!免得那些未受割礼的人来凌辱我。”但拿兵器的人非常害怕,不敢动手,扫罗就自己伏刀自尽。 5 拿兵器的人看见扫罗已死,也伏刀自尽了。 6 这样,扫罗和他的三个儿子及全家都死了。 7 住在山谷中的以色列人看见以色列军败逃、扫罗及其众子已死,都弃城而逃。于是,非利士人占领了那些城邑。 8 次日,非利士人来剥阵亡者的衣物,发现扫罗及其众子横尸基利波山, 9 就剥下扫罗的盔甲,割下他的头颅,并派人到非利士四境向他们的偶像和民众通告消息。 10 他们将扫罗的盔甲放在他们的神庙里,把他的头颅挂在大衮神庙中。 11 基列·雅比人听见非利士人对扫罗的所作所为, 12 他们所有的勇士就去把扫罗和他儿子们的尸体运到雅比,葬在雅比的橡树下,并禁食七天。 13 扫罗死了,因为他对耶和华不忠,不听从祂的教诲,甚至去求问灵媒, 14 而不求问耶和华。因此,耶和华使他被杀,把王位交给了耶西的儿子大卫。
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Chinese Contemporary Bible Copyright © 1979, 2005, 2007, 2011 by Biblica® Used by permission. All rights reserved worldwide.