1 Mafumu 9
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Yehova Aonekera Solomoni
9 Solomoni atatsiriza kumanga Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu, ndi kukwaniritsa kuchita zonse zimene ankafuna, 2 Yehova anamuonekera kachiwiri, monga momwe anamuonekera ku Gibiyoni. 3 Yehova ananena kwa iye kuti:
“Ndamva pemphero ndi pembedzero lako pa zimene wapempha pamaso panga. Ndayipatula Nyumba iyi, imene wamanga, poyikamo Dzina langa mpaka muyaya. Maso anga ndi mtima wanga zidzakhala pamenepo nthawi zonse.
4 “Kunena za iwe, ukayenda pamaso panga mokhulupirika, mwangwiro ndi moona mtima monga momwe anachitira abambo ako Davide, ndi kuchita zonse zimene ndakulamula ndi kusamalitsa malangizo ndi malamulo anga, 5 Ine ndidzakhazikitsa mpando wako waufumu pa Israeli mpaka muyaya, monga ndinalonjezera abambo ako Davide pamene ndinati, ‘Sipadzasowa munthu pa mpando waufumu wa Israeli.’
6 “Koma ngati iwe kapena ana ako mudzapatuka ndi kuleka kusunga malamulo ndi mawu anga amene ndakupatsani ndi kupita kukatumikira milungu ina ndi kuyipembedza, 7 pamenepo Ine ndidzazula Aisraeli mʼdziko limene ndinawapatsa ndiponso ndidzayikana Nyumba ino imene ndayipatula chifukwa cha Dzina langa. Pamenepo Aisraeli adzasanduka mwambi ndi chinthu chonyozedwa pakati pa anthu onse. 8 Ndipo ngakhale kuti tsopano Nyumba ya Mulunguyi ndi yokongola kwambiri, onse amene adzadutsa pano adzadabwa kwambiri ndipo adzatsonya ndipo adzati, ‘Nʼchifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere mʼdziko muno ndi pa Nyumba ya Mulunguyi?’ 9 Anthu adzayankha kuti, ‘Nʼchifukwa chakuti asiya Yehova Mulungu wawo amene anatulutsa makolo awo mʼdziko la Igupto, ndipo akangamira milungu ina ndi kumayipembedza ndi kuyitumikira. Choncho Iye wabweretsa zovuta zonsezi.’ ”
Zina zimene Solomoni Anachita
10 Patatha zaka makumi awiri, ndiye nthawi imene Solomoni anamanga nyumba ziwirizi: Nyumba ya Yehova ndi nyumba yaufumu, 11 Mfumu Solomoni anapereka mizinda makumi awiri ya ku Galileya kwa Hiramu mfumu ya ku Turo chifukwa Hiramu nʼkuti atapereka mitengo yonse ya mkungudza ndi ya payini ndiponso golide yense zimene Solomoni ankazifuna. 12 Koma Hiramu atabwera kuchokera ku Turo kudzaona mizinda imene Solomoni anamupatsa, sanasangalatsidwe nayo mizindayo. 13 Iye anafunsa kuti, “Mʼbale wanga, kodi iyi nʼkukhala mizinda yondipatsa?” Ndipo iye anayitcha mizindayo Dziko la Kabuli, dzina lomwe amatchedwa mpaka lero lino. 14 Koma Hiramu anali atatumiza kwa mfumu golide oposa makilogalamu 4,000.
15 Izi ndi zimene anachita Mfumu Solomoni: Analamula anthu kuti agwire ntchito yathangata pomanga Nyumba ya Yehova, nyumba yake, malo achitetezo a Milo, mpanda wa Yerusalemu, Hazori, Megido ndi Gezeri. 16 (Farao mfumu ya ku Igupto inali itathira nkhondo ndi kulanda Gezeri. Iye anatentha mzindawo. Anapha Akanaani amene ankakhala mʼmenemo ndipo kenaka anawupereka ngati mphatso yaukwati kwa mwana wake wamkazi amene anakwatiwa ndi Solomoni. 17 Ndipo Solomoni anamanganso Gezeri.) Iye anamanga Beti-Horoni Wakumunsi, 18 Baalati ndi Tadimori ku chipululu, mʼdziko lake lomwelo, 19 pamodzinso ndi mizinda yake yosungira chuma ndiponso mizinda yosungiramo magaleta ndi akavalo ake. Anamanganso chilichonse chimene anafuna kumanga ku Yerusalemu, ku Lebanoni ndi ku madera onse amene iye ankalamulira.
20 Panali anthu amene anatsala pakati pa mitundu ya Aamori, Ahiti, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi (anthu awa sanali Aisraeli). 21 Zimenezi ndiye zinali zidzukulu zawo zotsalira mʼdzikoli, anthu amene Aisraeli sanathe kuwawononga kotheratu. Solomoni anawatenga ndi kukhala akapolo ake ogwira ntchito yathangata, monga zilili mpaka lero lino. 22 Koma Solomoni sanagwiritse ntchito ya ukapolo Mwisraeli aliyense; iwo anali anthu ake ankhondo, nduna zake, atsogoleri a ankhondo, akapitawo ake, olamulira magaleta ndi oyendetsa magaleta ake. 23 Amenewa ndiwo anali akuluakulu oyangʼanira ntchito za Solomoni. Anthu okwana 550 ndiwo ankayangʼanira anthu amene ankagwira ntchitowo.
24 Mwana wamkazi wa Farao atachoka mu Mzinda wa Davide, kupita ku nyumba ya mfumu imene Solomoni anamumangira, Solomoni anamanga malo achitetezo a Milo.
25 Katatu pa chaka Solomoni ankapereka nsembe zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pa guwa lansembe limene anamangira Yehova ndiponso ankafukiza lubani pamaso pa Yehova. Potero ankakwaniritsa zoyenera kuchitika mu Nyumba ya Yehova.
26 Mfumu Solomoni anapanganso sitima zapamadzi ku Ezioni Geberi, malo amene ali pafupi ndi Eloti ku Edomu, mʼmbali mwa Nyanja Yofiira. 27 Ndipo Hiramu anatumiza anthu ake oyendetsa sitima zapamadzi amene ankadziwa za pa nyanja kuti aziyendetsa pamodzi ndi anthu a Solomoni. 28 Iwo anapita ku Ofiri ndipo anakatenga golide okwana makilogalamu 14,000, amene anamupereka kwa Mfumu Solomoni.
1 Kings 9
New International Version
The Lord Appears to Solomon(A)
9 When Solomon had finished(B) building the temple of the Lord and the royal palace, and had achieved all he had desired to do, 2 the Lord appeared(C) to him a second time, as he had appeared to him at Gibeon. 3 The Lord said to him:
“I have heard(D) the prayer and plea you have made before me; I have consecrated this temple, which you have built, by putting my Name(E) there forever. My eyes(F) and my heart will always be there.
4 “As for you, if you walk before me faithfully with integrity of heart(G) and uprightness, as David(H) your father did, and do all I command and observe my decrees and laws,(I) 5 I will establish(J) your royal throne over Israel forever, as I promised David your father when I said, ‘You shall never fail(K) to have a successor on the throne of Israel.’
6 “But if you[a] or your descendants turn away(L) from me and do not observe the commands and decrees I have given you[b] and go off to serve other gods(M) and worship them, 7 then I will cut off Israel from the land(N) I have given them and will reject this temple I have consecrated for my Name.(O) Israel will then become a byword(P) and an object of ridicule(Q) among all peoples. 8 This temple will become a heap of rubble. All[c] who pass by will be appalled(R) and will scoff and say, ‘Why has the Lord done such a thing to this land and to this temple?’(S) 9 People will answer,(T) ‘Because they have forsaken(U) the Lord their God, who brought their ancestors out of Egypt, and have embraced other gods, worshiping and serving them—that is why the Lord brought all this disaster(V) on them.’”
Solomon’s Other Activities(W)
10 At the end of twenty years, during which Solomon built these two buildings—the temple of the Lord and the royal palace— 11 King Solomon gave twenty towns in Galilee to Hiram king of Tyre, because Hiram had supplied him with all the cedar and juniper and gold(X) he wanted. 12 But when Hiram went from Tyre to see the towns that Solomon had given him, he was not pleased with them. 13 “What kind of towns are these you have given me, my brother?” he asked. And he called them the Land of Kabul,[d](Y) a name they have to this day. 14 Now Hiram had sent to the king 120 talents[e] of gold.(Z)
15 Here is the account of the forced labor King Solomon conscripted(AA) to build the Lord’s temple, his own palace, the terraces,[f](AB) the wall of Jerusalem, and Hazor,(AC) Megiddo and Gezer.(AD) 16 (Pharaoh king of Egypt had attacked and captured Gezer. He had set it on fire. He killed its Canaanite inhabitants and then gave it as a wedding gift to his daughter,(AE) Solomon’s wife. 17 And Solomon rebuilt Gezer.) He built up Lower Beth Horon,(AF) 18 Baalath,(AG) and Tadmor[g] in the desert, within his land, 19 as well as all his store cities(AH) and the towns for his chariots(AI) and for his horses[h]—whatever he desired to build in Jerusalem, in Lebanon and throughout all the territory he ruled.
20 There were still people left from the Amorites, Hittites,(AJ) Perizzites, Hivites and Jebusites(AK) (these peoples were not Israelites). 21 Solomon conscripted the descendants(AL) of all these peoples remaining in the land—whom the Israelites could not exterminate[i](AM)—to serve as slave labor,(AN) as it is to this day. 22 But Solomon did not make slaves(AO) of any of the Israelites; they were his fighting men, his government officials, his officers, his captains, and the commanders of his chariots and charioteers. 23 They were also the chief officials(AP) in charge of Solomon’s projects—550 officials supervising those who did the work.
24 After Pharaoh’s daughter(AQ) had come up from the City of David to the palace Solomon had built for her, he constructed the terraces.(AR)
25 Three(AS) times a year Solomon sacrificed burnt offerings and fellowship offerings on the altar he had built for the Lord, burning incense before the Lord along with them, and so fulfilled the temple obligations.
26 King Solomon also built ships(AT) at Ezion Geber,(AU) which is near Elath(AV) in Edom, on the shore of the Red Sea.[j] 27 And Hiram sent his men—sailors(AW) who knew the sea—to serve in the fleet with Solomon’s men. 28 They sailed to Ophir(AX) and brought back 420 talents[k] of gold,(AY) which they delivered to King Solomon.
Footnotes
- 1 Kings 9:6 The Hebrew is plural.
- 1 Kings 9:6 The Hebrew is plural.
- 1 Kings 9:8 See some Septuagint manuscripts, Old Latin, Syriac, Arabic and Targum; Hebrew And though this temple is now imposing, all
- 1 Kings 9:13 Kabul sounds like the Hebrew for good-for-nothing.
- 1 Kings 9:14 That is, about 4 1/2 tons or about 4 metric tons
- 1 Kings 9:15 Or the Millo; also in verse 24
- 1 Kings 9:18 The Hebrew may also be read Tamar.
- 1 Kings 9:19 Or charioteers
- 1 Kings 9:21 The Hebrew term refers to the irrevocable giving over of things or persons to the Lord, often by totally destroying them.
- 1 Kings 9:26 Or the Sea of Reeds
- 1 Kings 9:28 That is, about 16 tons or about 14 metric tons
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.