1 Akorinto 1
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
1 Paulo, woyitanidwa mwachifuniro cha Mulungu kuti akhale mtumwi wa Khristu Yesu ndi mʼbale wathu Sositene.
2 Kupita ku mpingo wa Mulungu ku Korinto, kwa oyeretsedwa mwa Khristu Yesu ndi oyitanidwa kukhala opatulika ndiponso kwa onse amene amapemphera mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu mʼdziko lonse lapansi, amene ndi Ambuye wawo ndi wathunso.
3 Landirani chisomo ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate athu ndi Ambuye athu Yesu Khristu.
Kuthokoza
4 Nthawi zonse ndimayamika Mulungu chifukwa cha inu chifukwa cha chisomo chake chopatsidwa kwa inu mwa Khristu Yesu. 5 Pakuti mwa Iye mwalemekezedwa mʼnjira iliyonse, mʼkuyankhula kwanu konse ndi mʼkudziwa kwanu konse, 6 chifukwa umboni wathu pa za Khristu unatsimikizidwa mwa inu. 7 Choncho inu simusowa mphatso yauzimu iliyonse pamene mukudikira mofunitsitsa kuti Ambuye athu Yesu Khristu avumbulutsidwe. 8 Adzakulimbikitsani mpaka kumapeto kuti mudzakhale wopanda mlandu pa tsiku lobwera Ambuye athu Yesu Khristu. 9 Mulungu amene wakuyitanani inu mu chiyanjano ndi Mwana wake Yesu Khristu Ambuye athu ngokhulupirika.
Kugawikana mu Mpingo
10 Ndidandaulira inu, abale, mʼdzina la Ambuye athu Yesu Khristu kuti nonsenu muvomerezane wina ndi mnzake kuti pasakhale kugawikana pakati panu ndi kuti mukhale amodzi kwenikweni mu nzeru ndi mʼmaganizo. 11 Abale anga, ena a ku nyumba ya Kloe andidziwitsa kuti pali mkangano pakati panu. 12 Chimene ndikutanthauza ndi ichi: wina amati, “Ndimatsatira Paulo,” wina, “Ndimatsatira Apolo,” wina, “Ndimatsatira Kefa,” winanso, “Ndimatsatira Khristu.”
13 Kodi Khristu wagawikana? Kodi Paulo anapachikidwa pa mtanda chifukwa cha inu? Kodi munabatizidwa mʼdzina la Paulo? 14 Ine ndikuyamika kuti sindinabatizepo mmodzi mwa inu kupatula Krispo ndi Gayo, 15 mwakuti palibe amene anganene kuti anabatizidwa mʼdzina langa. 16 (Inde, ine ndinabatizanso a mʼbanja la Stefano, koma sindikumbukira ngati ndinabatizanso wina aliyense). 17 Pakuti Khristu sananditume ine kudzabatiza, koma kudzalalikira Uthenga Wabwino, osati ndi mawu anzeru za umunthu, kuopa kuti mtanda wa Khristu ungakhale wopanda mphamvu.
Khristu ndiye Nzeru ndi Mphamvu za Mulungu
18 Pakuti uthenga wa mtanda ndi chopusa kwa iwo amene akuwonongeka, koma kwa ife amene tikupulumutsidwa uthengawu ndi mphamvu ya Mulungu. 19 Pakuti kwalembedwa kuti,
“Ine ndidzawononga nzeru za anthu anzeru;
luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
20 Munthu wanzeru ali kuti? Munthu wozama ndi maphunziro ali kuti? Munthu wodziwa zakuya zamakono ali kuti? Kodi Mulungu sanazipusitse nzeru za dziko lapansi? 21 Tsono poti mwa nzeru za Mulungu dziko lapansi mu nzeru zake silinamudziwe Iye, Mulungu amakondweretsedwa kuti kudzera mu chopusa cha zomwe zinalalikidwa apulumutse iwo amene akhulupirira. 22 Ayuda amafuna zizindikiro zodabwitsa ndipo Agriki amafunafuna nzeru, 23 koma ife timalalikira Khristu wopachikidwa. Chitsa chokhumudwitsa kwa Ayuda ndi chopusa kwa a mitundu ina. 24 Koma kwa iwo amene Mulungu anawayitana, Ayuda ndi Agriki omwe, Khristu ndi mphamvu ya Mulungu ndi nzeru za Mulungu. 25 Pakuti za Mulungu zooneka ngati zopusa, ndi za nzeru kuposa nzeru za munthu, ndipo za Mulungu zooneka ngati zofowoka, zili ndi mphamvu kuposa mphamvu za munthu.
26 Abale taganizirani mmene munalili musanayitanidwe. Si ambiri a inu munali a nzeru, si ambiri a inu munali a mphamvu zamakopedwe. Si ambiri a inu munali obadwa pa ulemerero. 27 Koma Mulungu anasankha zinthu zopusa za dziko lapansi kuti achititse manyazi anzeru. Mulungu anasankha zinthu zofowoka za dziko lapansi kuti achititse manyazi amphamvu. 28 Anasankha zinthu zapansipansi ndi zopeputsidwa za dziko la pansi lino, zinthu zimene kulibe, kuti asukulutse zimene zilipo, 29 kuti munthu asanyade pamaso pa Mulungu. 30 Nʼchifukwa cha Iye kuti inu muli mwa Khristu Yesu, amene wakhala nzeru ya kwa Mulungu, kwa ife, kunena kuti kulungama kwathu, chiyero ndi chipulumutso. 31 Choncho poti zinalembedwa kuti, “Ngati munthu akufuna kunyadira, anyadire mwa Ambuye.”
哥林多前书 1
Chinese Contemporary Bible (Simplified)
问候
1 我是按上帝旨意蒙召做基督耶稣使徒的保罗,同所提尼弟兄, 2 写信给在哥林多的上帝的教会,就是在基督耶稣里得以圣洁、蒙召做圣徒的,以及各地求告我们主耶稣基督之名的人。基督是他们的主,也是我们的主。
3 愿我们的父上帝和主耶稣基督赐给你们恩典和平安!
保罗的感恩
4 我常常为你们感谢我的上帝,因为祂在基督耶稣里赐给了你们恩典, 5 使你们在基督里凡事富足,有全备的口才和知识。 6 这样,我为基督所做的见证就在你们身上得到了证实。 7 因此,你们在殷切等候我们主耶稣基督再来的期间,并不缺少任何属灵的恩赐。 8 我们的主耶稣基督必扶持你们到底,使你们在祂再来的日子无可指责。 9 上帝是信实的,祂呼召你们是要你们与祂的儿子——我们的主耶稣基督相交。
信徒要同心合意
10 亲爱的弟兄姊妹,我奉主耶稣基督的名劝你们,要同心合意,不可结党纷争,要团结一致, 11 因为革来家的人把各位弟兄姊妹的事情告诉了我,说你们中间有纷争。 12 我的意思是你们有人说:“我是跟随保罗的”,有人说:“我是跟随亚波罗的”,有人说:“我是跟随彼得的”,有人说:“我是跟随基督的”。 13 难道基督是分成几派的吗?替你们钉十字架的是保罗吗?你们是奉保罗的名受洗的吗?
14 感谢上帝,除了基利司布和该犹以外,我没有为你们任何人施洗, 15 所以没有人能说是奉我的名受洗的。 16 不错,我也曾为司提法纳的家人施洗,除此以外,我不记得还为谁施洗了。 17 基督不是差遣我去为人施洗,而是去传扬福音,而且不用高言大智,免得基督十字架的能力被抹杀。
上帝的智慧
18 因为十字架之道在将要灭亡的人看来是愚昧的,但对我们这些得救的人来说却是上帝的大能, 19 正如圣经上说:“我要摧毁智者的智慧,废弃明哲的聪明。”
20 这个世代所谓的智者、学者、雄辩家在哪里?上帝岂不是把这世上的智慧都变成愚昧了吗? 21 上帝运用自己的智慧不让世人凭自己的智慧去认识祂,祂乐意采用世人看为愚昧的道理去拯救那些相信的人,这就是上帝的智慧。
22 犹太人要看神迹,希腊人寻求智慧, 23 但我们传讲被钉十字架的基督。这对犹太人来说是绊脚石,对外族人来说是愚昧的。 24 但对于蒙召的人,无论是犹太人还是希腊人,基督是上帝的能力、上帝的智慧。 25 因为上帝的“愚昧”也胜过世人的智慧,上帝的“软弱”也胜过世人的刚强。
26 弟兄姊妹,想想你们蒙召时的情形。按人的标准来衡量,你们当中称得上有智慧的不多,有能力的不多,出身名门望族的也不多。 27 但上帝拣选了世人看为愚昧的,要使智者羞愧;上帝拣选了世上软弱的,要使强者蒙羞; 28 上帝拣选了世上卑贱的、被藐视的和无足轻重的,要使世人看为举足轻重的变得无足轻重。 29 这样,谁都不能在上帝面前自夸了。
30 上帝使你们活在基督耶稣里,祂使基督耶稣成为我们的智慧、公义、圣洁和救赎。 31 所以,正如圣经上说:“要夸耀,就当夸耀主的作为。”
哥林多前書 1
Chinese Contemporary Bible (Traditional)
問候
1 我是按上帝旨意蒙召作基督耶穌使徒的保羅,同所提尼弟兄, 2 寫信給在哥林多的上帝的教會,就是在基督耶穌裡得以聖潔、蒙召做聖徒的,以及各地求告我們主耶穌基督之名的人。基督是他們的主,也是我們的主。
3 願我們的父上帝和主耶穌基督賜給你們恩典和平安!
保羅的感恩
4 我常常為你們感謝我的上帝,因為祂在基督耶穌裡賜給了你們恩典, 5 使你們在基督裡凡事富足,有全備的口才和知識。 6 這樣,我為基督所做的見證就在你們身上得到了證實。 7 因此,你們在殷切等候我們主耶穌基督再來的期間,並不缺少任何屬靈的恩賜。 8 我們的主耶穌基督必扶持你們到底,使你們在祂再來的日子無可指責。 9 上帝是信實的,祂呼召你們是要你們與祂的兒子——我們的主耶穌基督相交。
信徒要同心合意
10 親愛的弟兄姊妹,我奉主耶穌基督的名勸你們,要同心合意,不可結黨紛爭,要團結一致, 11 因為革來家的人把各位弟兄姊妹的事情告訴了我,說你們中間有紛爭。 12 我的意思是你們有人說:「我是跟隨保羅的」,有人說:「我是跟隨亞波羅的」,有人說:「我是跟隨彼得的」,有人說:「我是跟隨基督的」。 13 難道基督是分成幾派的嗎?替你們釘十字架的是保羅嗎?你們是奉保羅的名受洗的嗎?
14 感謝上帝,除了基利司布和該猶以外,我沒有為你們任何人施洗, 15 所以沒有人能說是奉我的名受洗的。 16 不錯,我也曾為司提法納的家人施洗,除此以外,我不記得還為誰施洗了。 17 基督不是差遣我去為人施洗,而是去傳揚福音,而且不用高言大智,免得基督十字架的能力被抹摋。
上帝的智慧
18 因為十字架之道在將要滅亡的人看來是愚昧的,但對我們這些得救的人來說卻是上帝的大能, 19 正如聖經上說:「我要摧毀智者的智慧,廢棄明哲的聰明。」
20 這個世代所謂的智者、學者、雄辯家在哪裡?上帝豈不是把這世上的智慧都變成愚昧了嗎? 21 上帝運用自己的智慧不讓世人憑自己的智慧去認識祂,祂樂意採用世人看為愚昧的道理去拯救那些相信的人,這就是上帝的智慧。
22 猶太人要看神蹟,希臘人尋求智慧, 23 但我們傳講被釘十字架的基督。這對猶太人來說是絆腳石,對外族人來說是愚昧的。 24 但對於蒙召的人,無論是猶太人還是希臘人,基督是上帝的能力、上帝的智慧。 25 因為上帝的「愚昧」也勝過世人的智慧,上帝的「軟弱」也勝過世人的剛強。
26 弟兄姊妹,想想你們蒙召時的情形。按人的標準來衡量,你們當中稱得上有智慧的不多,有能力的不多,出身名門望族的也不多。 27 但上帝揀選了世人看為愚昧的,要使智者羞愧;上帝揀選了世上軟弱的,要使強者蒙羞; 28 上帝揀選了世上卑賤的、被藐視的和無足輕重的,要使世人看為舉足輕重的變得無足輕重。 29 這樣,誰都不能在上帝面前自誇了。
30 上帝使你們活在基督耶穌裡,祂使基督耶穌成為我們的智慧、公義、聖潔和救贖。 31 所以,正如聖經上說:「要誇耀,就當誇耀主的作為。」
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Chinese Contemporary Bible Copyright © 1979, 2005, 2007, 2011 by Biblica® Used by permission. All rights reserved worldwide.