約伯記 41
Chinese Union Version Modern Punctuation (Traditional)
神萬能人難仰望
41 「你能用魚鉤釣上鱷魚嗎?能用繩子壓下牠的舌頭嗎? 2 你能用繩索穿牠的鼻子嗎?能用鉤穿牠的腮骨嗎? 3 牠豈向你連連懇求,說柔和的話嗎? 4 豈肯與你立約,使你拿牠永遠做奴僕嗎? 5 你豈可拿牠當雀鳥玩耍嗎?豈可為你的幼女將牠拴住嗎? 6 搭夥的漁夫豈可拿牠當貨物嗎?能把牠分給商人嗎? 7 你能用倒鉤槍扎滿牠的皮,能用魚叉叉滿牠的頭嗎? 8 你按手在牠身上,想與牠爭戰,就不再這樣行吧。 9 人指望捉拿牠是徒然的,一見牠,豈不喪膽嗎? 10 沒有那麼凶猛的人敢惹牠。這樣,誰能在我面前站立得住呢? 11 誰先給我什麼,使我償還呢?天下萬物都是我的。
12 「論到鱷魚的肢體和其大力,並美好的骨骼,我不能緘默不言。 13 誰能剝牠的外衣?誰能進牠上下牙骨之間呢? 14 誰能開牠的腮頰?牠牙齒四圍是可畏的。 15 牠以堅固的鱗甲為可誇,緊緊合閉,封得嚴密。 16 這鱗甲一一相連,甚至氣不得透入其間, 17 都是互相聯絡,膠結不能分離。 18 牠打噴嚏就發出光來,牠眼睛好像早晨的光線[a]。 19 從牠口中發出燒著的火把,與飛迸的火星。 20 從牠鼻孔冒出煙來,如燒開的鍋和點著的蘆葦。 21 牠的氣點著煤炭,有火焰從牠口中發出。 22 牠頸項中存著勁力,在牠面前的都恐嚇蹦跳。 23 牠的肉塊互相聯絡,緊貼其身,不能搖動。 24 牠的心結實如石頭,如下磨石那樣結實。 25 牠一起來,勇士都驚恐,心裡慌亂,便都昏迷。 26 人若用刀,用槍,用標槍,用尖槍扎牠,都是無用。 27 牠以鐵為乾草,以銅為爛木。 28 箭不能恐嚇牠使牠逃避,彈石在牠看為碎秸。 29 棍棒算為禾秸,牠嗤笑短槍颼的響聲。 30 牠肚腹下如尖瓦片,牠如釘耙經過淤泥。 31 牠使深淵開滾如鍋,使洋海如鍋中的膏油。 32 牠行的路隨後發光,令人想深淵如同白髮。 33 在地上沒有像牠造的那樣,無所懼怕。 34 凡高大的,牠無不藐視,牠在驕傲的水族上做王。」
Footnotes
- 約伯記 41:18 「光線」原文作「眼皮」。
Yobu 41
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
41 “Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba
kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
2 Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake,
kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
3 Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo?
Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
4 Kodi idzachita nawe mgwirizano
kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
5 Kodi udzasewera nayo ngati mbalame,
kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
6 Kodi anthu adzayitsatsa malonda?
Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
7 Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga,
kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
8 Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo,
ndipo iweyo sudzabwereranso.
9 Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza;
kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa.
Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere?
Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
12 “Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho,
za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
13 Ndani angasende chikopa chake?
Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
14 Ndani angatsekule kukamwa kwake,
pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 Kumsana kwake kuli mizere ya mamba
onga zishango zolumikizanalumikizana;
16 Mambawo ndi olukanalukana
kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
17 Ndi olumikizanalumikizana;
ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali;
maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
19 Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo
mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi
ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
21 Mpweya wake umayatsa makala,
ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
22 Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake;
aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
23 Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo
ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
24 Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala,
ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 Ngʼonayo ikangovuwuka,
ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu,
ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
27 Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe
ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
28 Muvi sungathe kuyithawitsa,
miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
29 Zibonga zimakhala ngati ziputu;
imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
30 Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo
imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
31 Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali,
imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
32 Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee,
kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
33 Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho,
nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 Chimanyoza nyama zina zonse;
icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”
Copyright © 2011 by Global Bible Initiative
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.