Add parallel Print Page Options

Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzatuma mthenga wanga amene adzakonza njira pamaso panga. Kenaka mwadzidzidzi Ambuye amene mukumufunafuna adzafika ku Nyumba yake. Mthenga wapangano amene mukumuyembekezera adzabwera.”

Koma ndani adzatha kupirira pa tsiku la kubwera kwake? Ndani adzatha kuyima pamene Iye wafika? Pakuti adzakhala ngati moto wa mmisiri wa pa ngʼanjo, kapenanso ngati sopo wa munthu wochapa. Iye adzachita kukhalira pansi ngati mmisiri woyenga ndi woyeretsa siliva. Iye adzayeretsa Alevi ndi kuwayenga ngati golide ndi siliva. Pamenepo Yehova adzakhala ndi anthu amene azidzabweretsa zopereka mwachilungamo, ndipo Yehova adzalandira zopereka za Yuda ndi Yerusalemu, ngati masiku akale, masiku amakedzana.

Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Tsono ndidzakuyandikirani kuti ndikuweruzeni. Mosataya nthawi ndidzanena mawu otsutsa mfiti, achigololo, a umboni wonama, amene salipira bwino antchito awo, amene amazunza akazi ndi ana amasiye, amene saweruza alendo mwachilungamo, komanso amene sandiopa Ine.”

Kuba za Mulungu

“Ine ndine Yehova, ndipo sindisintha. Choncho inu zidzukulu za Yakobo, simunawonongedwe. Kuyambira nthawi ya makolo anu mwakhala mukuphwanya malamulo anga ndipo simunawatsatire. Bwererani kwa Ine, ndipo Ine ndidzabwerera kwa inu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

“Koma inu mukufunsa kuti, ‘Tibwerere motani kwa Yehova?’

“Kodi munthu angathe kuba za Mulungu? Komatu inu mumandibera.

“Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi timakuberani motani?’

“Pa zakhumi ndi pa zopereka. Mtundu wanu wonse ndinu otembereredwa, chifukwa mukundibera. 10 Bweretsani chakhumi chathunthu ku nyumba yosungira, kuti mukhale chakudya mʼnyumba mwanga.” Akutero Yehova Wamphamvuzonse, “Tandiyesani, ndipo muone ngati sindidzatsekula zipata zakumwamba, ndi kukugwetserani madalitso ochuluka amene mudzasowe malo owayikamo. 11 Ndidzaletsa tizirombo kuti tisawononge mbewu zanu, ndipo mpesa wa mʼminda mwanu zipatso zake sizidzayoyoka,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. 12 “Motero anthu amitundu yonse adzakutchulani odala, pakuti dziko lanu lidzakhala lokondweretsa,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.

13 Yehova akuti, “Mwayankhula mawu owawa onena za Ine.

“Komabe inu mukufunsa kuti, ‘Kodi tanena chiyani chotsutsana nanu?’

14 “Mwanena kuti, ‘Kutumikira Mulungu nʼkosapindulitsa. Kodi timapindulanji pochita zofuna zake, ndi kumayenda ngati anamfedwa pamaso pa Yehova Wamphamvuzonse? 15 Koma tsono ife timati anthu odzikuza ndiye odalitsika. Kunena zoona anthu oyipa ndiye amapeza bwino, ngakhale amene amanyoza Mulungu amapulumuka.’ ”

16 Ndipo woopa Yehova anayamba kukambirana, ndipo Yehova anamvetsera. Buku la chikumbutso linalembedwa pamaso pake, lonena za amene amaopa Yehova ndi kulemekeza dzina lake.

17 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Anthu amenewo adzakhala anga, tsiku limene Ine ndidzachita izi, adzakhala angaanga. Ndidzawaleka osawalanga monga mmene munthu amachitira chifundo mwana wake amene amamutumikira. 18 Pamenepo mudzaonanso kusiyana pakati pa anthu olungama ndi oyipa, pakati pa amene amatumikira Mulungu ndi amene satumikira Mulungu.”

The Coming Messenger

“Behold, (A)I send My messenger,
And he will (B)prepare the way before Me.
And the Lord, whom you seek,
Will suddenly come to His temple,
(C)Even the Messenger of the covenant,
In whom you delight.
Behold, (D)He is coming,”
Says the Lord of hosts.

“But who can endure (E)the day of His coming?
And (F)who can stand when He appears?
For (G)He is like a refiner’s fire
And like launderers’ soap.
(H)He will sit as a refiner and a purifier of silver;
He will purify the sons of Levi,
And [a]purge them as gold and silver,
That they may (I)offer to the Lord
An offering in righteousness.

“Then (J)the offering of Judah and Jerusalem
Will be [b]pleasant to the Lord,
As in the days of old,
As in former years.
And I will come near you for judgment;
I will be a swift witness
Against sorcerers,
Against adulterers,
(K)Against perjurers,
Against those who (L)exploit wage earners and (M)widows and orphans,
And against those who turn away an alien—
Because they do not fear Me,”
Says the Lord of hosts.

“For I am the Lord, (N)I do not change;
(O)Therefore you are not consumed, O sons of Jacob.
Yet from the days of (P)your fathers
You have gone away from My ordinances
And have not kept them.
(Q)Return to Me, and I will return to you,”
Says the Lord of hosts.
(R)“But you said,
‘In what way shall we return?’

Do Not Rob God

“Will a man rob God?
Yet you have robbed Me!
But you say,
‘In what way have we robbed You?’
(S)In tithes and offerings.
You are cursed with a curse,
For you have robbed Me,
Even this whole nation.
10 (T)Bring all the tithes into the (U)storehouse,
That there may be food in My house,
And try Me now in this,”
Says the Lord of hosts,
“If I will not open for you the (V)windows of heaven
And (W)pour out for you such blessing
That there will not be room enough to receive it.

11 “And I will rebuke (X)the devourer for your sakes,
So that he will not destroy the fruit of your ground,
Nor shall the vine fail to bear fruit for you in the field,”
Says the Lord of hosts;
12 “And all nations will call you blessed,
For you will be (Y)a delightful land,”
Says the Lord of hosts.

The People Complain Harshly

13 “Your(Z) words have been [c]harsh against Me,”
Says the Lord,
“Yet you say,
‘What have we spoken against You?’
14 (AA)You have said,
‘It is useless to serve God;
What profit is it that we have kept His ordinance,
And that we have walked as mourners
Before the Lord of hosts?
15 So now (AB)we call the proud blessed,
For those who do wickedness are [d]raised up;
They even (AC)tempt God and go free.’ ”

A Book of Remembrance

16 Then those (AD)who feared the Lord (AE)spoke to one another,
And the Lord listened and heard them;
So (AF)a book of remembrance was written before Him
For those who fear the Lord
And who [e]meditate on His name.

17 “They(AG) shall be Mine,” says the Lord of hosts,
“On the day that I make them My (AH)jewels.[f]
And (AI)I will spare them
As a man spares his own son who serves him.”
18 (AJ)Then you shall again discern
Between the righteous and the wicked,
Between one who serves God
And one who does not serve Him.

Footnotes

  1. Malachi 3:3 Or refine
  2. Malachi 3:4 pleasing
  3. Malachi 3:13 Lit. strong
  4. Malachi 3:15 Lit. built
  5. Malachi 3:16 Or esteem
  6. Malachi 3:17 Lit. special treasure