耶和華的日子

14 看啊,耶和華的日子快到了,那時你那裡的財物必被搶掠、瓜分。 因為我必招聚萬國去攻打耶路撒冷。那時,城必失守,房屋必被洗劫,婦女必被玷污。半城的人必被擄去,剩下的人必留在城中,不會被剷除。 那時,耶和華必出來與列國爭戰,像從前爭戰的日子一樣。 到那天,祂的腳必踏在耶路撒冷東面的橄欖山上,這山必從東至西分成兩半,一半向北移,一半向南移,中間形成極大的山谷。 你們要從我的這山谷逃跑,因為山谷必延伸到亞薩。你們必像猶大王烏西雅年間的人躲避大地震一樣逃跑。我的上帝耶和華必帶著所有的聖者降臨。 到那天,將沒有光、嚴寒和冰霜。 那將是奇特的日子,沒有晝夜之分,晚上仍然有光,只有上帝知道那日何時來臨。

到那天,必有活水從耶路撒冷湧出,一半流向死海,一半流向地中海,冬夏不變。 耶和華必做普世的王。到那天,必唯祂獨尊,唯祂的名獨尊。 10 從迦巴直到耶路撒冷南邊的臨門,整個地區都要變為平原。從便雅憫門到舊門,再到角門,從哈楠業樓到王的榨酒池——耶路撒冷必仍然矗立在原處。 11 城內必有人居住,不再遭毀滅的咒詛。耶路撒冷必安享太平。

12 耶和華必降瘟疫給攻打耶路撒冷的列邦,使他們活著的時候皮肉已經腐爛,眼睛在眼眶中腐爛,舌頭在口中腐爛。 13 到那天,耶和華必使他們慌亂不堪,彼此揪住,互相毆打。 14 猶大也必在耶路撒冷爭戰,四圍列國的財物——大量的金銀和衣服必被收聚起來。 15 同樣的瘟疫也必降在馬匹、騾子、駱駝、驢和營中的其他牲畜身上。

16 前來攻打耶路撒冷的列國中的倖存者,必每年上來敬拜大君王——萬軍之耶和華,並且守住棚節。 17 地上萬族中若有人不上耶路撒冷敬拜大君王——萬軍之耶和華,他們必沒有雨水。 18 埃及人若不上來敬拜,也必沒有雨水,耶和華必使他們和不上來守住棚節的列國一樣遭受瘟疫。 19 這將是埃及和不上來守住棚節的列國所得的懲罰。 20 到那天,馬鈴上也必刻上「獻給耶和華」的字樣。耶和華殿內的鍋必像祭壇前的碗一樣聖潔。 21 耶路撒冷和猶大的鍋都是萬軍之耶和華的聖物,來獻祭的人都可以用這些鍋煮祭肉。到那天,萬軍之耶和華的殿中必再也沒有商人。

Yehova Akubwera ndipo Akulamulira

14 Taonani tsiku la Yehova likubwera pamene zinthu zimene adani ako anakulanda azidzagawana iwe ukuona.

Ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse kuti adzathire nkhondo Yerusalemu; mzindawu udzalandidwa, nyumba zidzaphwasulidwa, ndipo akazi adzagwiriridwa. Theka la anthu a mu mzindamu lidzapita ku ukapolo, koma ena onse otsala mu mzindamu sadzachotsedwa.

Pamenepo Yehova adzabwera kudzamenyana ndi mitundu ya anthu imeneyi, ngati mmene amachitira pa nthawi ya nkhondo. Tsiku limenelo adzayimirira pa Phiri la Olivi, kummawa kwa Yerusalemu, ndipo Phiri la Olivilo lidzagawikana pawiri kuyambira kummawa mpaka kumadzulo, kupanga chigwa chachikulu, kuchititsa kuti theka la phiri lisunthire kumpoto ndi linalo kummwera. Inu mudzathawa podzera mʼchigwa chapakati pa phirilo, pakuti chidzafika mpaka ku Azeli. Mudzathawa monga munachitira pa tsiku la chivomerezi nthawi ya Uziya mfumu ya Yuda. Kenaka Yehova Mulungu wanga adzabwera, pamodzi ndi oyera ake onse.

Tsiku limenelo sipadzakhala kuwala, kuzizira kapena chisanu. Lidzakhala tsiku lapaderadera, silidzakhala usana kapena usiku; tsiku limeneli akulidziwa ndi Yehova yekha. Ikadzafika nthawi ya madzulo, kudzakhala kukuwalabe.

Tsiku limenelo madzi amoyo adzatuluka mu Yerusalemu, theka lidzapita ku nyanja ya kummawa ndipo theka lina ku nyanja ya kumadzulo, nthawi yachilimwe ndi nthawi yozizira yomwe.

Ndipo Yehova adzakhala mfumu pa dziko lonse lapansi. Tsiku limenelo padzakhala Ambuye mmodzi yekha, ndipo dzina lidzakhala limodzi lomwelo.

10 Dziko lonse, kuyambira ku Geba mpaka ku Rimoni, kummwera kwa Yerusalemu, lidzakhala ngati Araba. Koma Yerusalemu adzakwezedwa ndipo adzakhala pamalo pakepo, kuyambira ku Chipata cha Benjamini mpaka ku malo amene ali ku Chipata Choyamba, ku Chipata Chapangodya, ndipo kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku malo opsinyira mphesa za mfumu. 11 Mʼmenemo mudzakhala anthu; sadzawonongedwanso. Yerusalemu adzakhala pa mtendere.

12 Mliri umene Yehova adzakanthire nawo mitundu yonse ya anthu imene inkamenyana ndi Yerusalemu ndi uwu: Matupi awo adzawola iwo eni akuyenda, maso awo adzawola ali mʼmalo mwake, ndipo malilime awo adzawola ali mʼkamwa mwawo. 13 Pa tsiku limenelo Yehova adzasokoneza anthu akuluakulu. Munthu aliyense adzagwira dzanja la mnzake, ndi kuyamba kumenyana okhaokha. 14 Yuda nayenso adzachita nkhondo ku Yerusalemu. Chuma chonse cha anthu a mitundu yozungulira adzachisonkhanitsa pamodzi; golide, siliva ndi zovala zochuluka kwambiri. 15 Mliri womwewo udzapha akavalo ndi nyulu, ngamira ndi abulu, pamodzi ndi nyama zonse zokhala ku misasako.

16 Kenaka opulumuka ochokera mwa mitundu yonse ya anthu amene anathira nkhondo Yerusalemu, azidzapita chaka ndi chaka kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, ndiponso kukachita Chikondwerero cha Misasa. 17 Ngati mitundu ina ya anthu pa dziko lapansi sidzapita ku Yerusalemu kukapembedza Mfumu Yehova Wamphamvuzonse, idzakhala wopanda mvula. 18 Ndipo ngati anthu a ku Igupto sadzapita ndi kukakhala nawo kumeneko, adzakhala wopanda mvula. Yehova adzabweretsa pa iwo mliri umene analangira mitundu ina ya anthu imene sinapite ku Chikondwerero cha Misasa. 19 Chimenechi chidzakhala chilango cha Igupto ndiponso mitundu ina yonse imene sidzapita ku Chikondwerero cha Misasa.

20 Pa tsiku limenelo pa maberu a akavalo padzalembedwa mawu oti wopatulikira Yehova, ndipo miphika ya mʼNyumba ya Yehova idzakhala yopatulika ngati mbale za ku guwa. 21 Mʼphika uliwonse ku Yerusalemu ndi ku Yuda udzakhala wopatulikira Yehova Wamphamvuzonse, ndipo onse amene adzabwera kudzapereka nsembe adzatenga miphika ina ndi kuphikiramo. Ndipo nthawi imeneyo simudzakhalanso Akanaani mʼNyumba ya Yehova Wamphamvuzonse.