弥迦书 3
Chinese New Version (Traditional)
指摘官長與領袖
3 我說:
“雅各的首領,你們要聽,
以色列家的官長,你們也要聽;
難道你們不知道公平嗎?
2 然而,你們恨惡良善,喜愛邪惡,
從人身上剝皮,
從人骨頭上剔肉。
3 你們吃我民的肉,
剝他們的皮,
打斷他們的骨頭,
切成像鍋裡的塊,
像釜中的肉塊。
4 那時,他們要向耶和華呼求,
耶和華卻不應允他們。
到那時,耶和華必掩面不顧他們,
因為他們行了惡事。”
責備假先知
5 關於那些使我民走迷路的先知,
耶和華這樣說:
“他們的牙齒有所咀嚼的時候,
就大叫‘平安’;
誰不把食物給他們吃,
他們就攻擊那人。”
6 因此你們只有黑夜,沒有異象,
只有黑暗,沒有默示。
對先知,日頭要下落,
為他們,白日變為黑暗。
7 先見必抱愧,
得默示的人要蒙羞;
他們都必掩著上唇,
因為沒有 神的答覆。
8 至於我,我卻藉著耶和華的靈,
滿有力量、公平和能力,
可以向雅各述說他的過犯,
向以色列指出他的罪惡。
惡有惡報─聖城被毀
9 雅各家的首領,你們要聽這個,
以色列家的官長,你們也要聽;
你們厭惡公平,
屈枉正直,
10 用人血建錫安,
以罪孽造耶路撒冷。
11 城中的首領為賄賂而審判,
祭司為薪俸而教導,
先知為銀子說默示,
他們竟倚靠耶和華,說:
“耶和華不是在我們中間嗎?
災禍必不會臨到我們身上。”
12 所以,為你們的緣故,
錫安必像被耕種的田地,
耶路撒冷必變為亂堆,
這殿的山要成為叢林中的高岡。
Mika 3
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Atsogoleri ndi Aneneri Adzudzulidwa
3 Ndipo ine ndinati,
“Tamverani, inu atsogoleri a Yakobo,
inu olamulira nyumba ya Israeli.
Kodi sindinu oyenera kudziwa kuweruza molungama,
2 inu amene mumadana ndi zabwino ndi kukonda zoyipa;
inu amene mumasenda khungu la anthu anga,
ndipo mumakungunula mnofu pa mafupa awo;
3 inu amene mumadya anthu anga,
mumasenda khungu lawo
ndi kuphwanya mafupa awo;
inu amene mumawadula nthulinthuli
ngati nyama yokaphika?”
4 Pamenepo adzalira kwa Yehova,
koma Iye sadzawayankha.
Nthawi imeneyo Iye adzawabisira nkhope yake
chifukwa cha zoyipa zimene anazichita.
5 Yehova akuti,
“Aneneri amene
amasocheretsa anthu anga,
ngati munthu wina awapatsa chakudya
amamufunira ‘mtendere;’
ngati munthu wina sawapatsa zakudya
amamulosera zoyipa.
6 Nʼchifukwa chake kudzakuderani,
simudzaonanso masomphenya,
mdima udzakugwerani ndipo simudzawombezanso.
Dzuwa lidzawalowera aneneriwo, ndipo mdima udzawagwera.
7 Alosi adzachita manyazi
ndipo owombeza mawula adzanyazitsidwa.
Onse adzaphimba nkhope zawo
chifukwa Mulungu sakuwayankha.”
8 Koma kunena za ine, ndadzazidwa ndi mphamvu,
ndi Mzimu wa Yehova,
ndi kulungama, ndi kulimba mtima,
kuti ndilalikire za kugalukira kwa Yakobo,
kwa Israeli za tchimo lake.
9 Imvani izi, inu atsogoleri a nyumba ya Yakobo,
inu olamulira nyumba ya Israeli,
inu amene mumadana ndi kuweruza kolungama;
ndipo mumakhotetsa zinthu zonse zolondola;
10 inu amene mukumanga Ziyoni pokhetsa magazi,
ndi Yerusalemu ndi kuyipa kwanu.
11 Atsogoleri ake amalandira chiphuphu kuti aweruze,
ansembe ake amalandira malipiro kuti alalikire,
ndipo aneneri ake amanenera kuti alandire ndalama.
Komatu amatsamira pa Yehova nʼkumanena kuti,
“Kodi Yehova sali pakati pathu?
Palibe tsoka limene lidzatigwere.”
12 Choncho chifukwa cha inu,
Ziyoni adzatipulidwa ngati munda,
Yerusalemu adzasanduka bwinja,
ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.
Chinese New Version (CNV). Copyright © 1976, 1992, 1999, 2001, 2005 by Worldwide Bible Society.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
