Add parallel Print Page Options

我自己决定了,到你们那里去的时候,不再是忧愁的。 如果我使你们忧愁,除了那因我而忧愁的人以外,谁能使我快乐呢? 我写了这样的信,免得我来的时候,应该使我快乐的人反而使我忧愁;我深信你们众人都以我的喜乐为你们的喜乐。 我从前心里痛苦难过,流着眼泪写信给你们,并不是要使你们忧愁,而是要你们知道我是多么爱你们。

饶恕犯罪的弟兄

如果有人使人忧愁,他不是使我忧愁,而是使你们众人都有一点忧愁;我只说有一点,是避免说得过分。 这样的人受了许多人的责备,也就够了, 倒不如饶恕他,安慰他,免得他因忧愁过度而受不了。 所以,我劝你们要向他确实显明你们的爱心。 为这缘故,我写了那封信,要考验你们是不是凡事都顺从。 10 你们饶恕谁,我也饶恕谁;我所饶恕了的(如果我饶恕过甚么),是为了你们在基督面前饶恕的, 11 免得撒但有机可乘,因为我们并不是不晓得他的诡计。

基督的馨香

12 从前我为基督的福音到了特罗亚,虽然主给我开了门, 13 我心里仍然没有安宁,因为见不到提多弟兄。于是我辞别了那里的人,到马其顿去了。

14 感谢 神,他常常在基督里,使我们这些作俘虏的,列在凯旋的队伍当中,又借着我们在各地散播香气,就是使人认识基督。 15 因为无论在得救的人或灭亡的人中间,我们都是基督的馨香,是献给 神的。 16 对于灭亡的人,这是死亡的气味叫人死;对于得救的人,这却是生命的香气使人活。这些事谁够资格作呢? 17 我们不像那许多的人,为了图利而谬讲 神的道。相反地,我们讲话,是出于真诚,出于 神,是在 神面前、在基督里的。

Kotero ndinatsimikiza maganizo anga kuti ndisachitenso ulendo wina owawa wobwera kwanuko. Pakuti ngati ndikumvetsani chisoni, kodi angandisangalatse ndani, kupatula inuyo amene ndakumvetsani chisoni? Nʼchifukwa chake ndinakulemberani monga ndinachitiramo kuti nditabwera kwanuko ndisadzamve chisoni ndi anthu oyenera kundisangalatsa. Ndinali ndi chikhulupiriro ndi inu nonse kuti inuyo mukakhala ndi chimwemwe poona kuti inenso ndili ndi chimwemwe. Pakuti ndinakulemberani kalata ija ndili wopsinjika ndi wowawidwa mtima kwambiri ndi kutuluka misozi yambiri, osati pofuna kukumvetsani chisoni koma kuti ndikudziwitseni kuti ndimakukondani kwambiri.

Za Kukhululukira Wolakwa

Koma ngati wina wamvetsa chisoni, sanamvetse chisoni ine ndekha, koma koposa mosawonjezera wakhumudwitsa nonsenu, kunenatu mosawonjezera. Chilango chimene ambiri a inu mwamupatsa munthu ameneyu nʼchokwanira. Mʼmalo mwake tsono, muyenera kumukhululukira ndi kumulimbikitsa mtima kuti asamve chisoni choposa muyeso, angataye mtima. Choncho ndikukupemphani kuti mutsimikizire chikondi chanu pa iye. Cholinga china chimene ndinakulemberani kalata ija chinali chofuna kukuonani ngati mudzandimvera pa zonse. 10 Aliyense amene mumukhululukire, inenso ndimukhululukira. Ndipo ndikakhululukira, ngati pali kanthu koti ndikhululukire, ndiye kuti ndakhululuka chifukwa cha inu pamaso pa Khristu, 11 kupewa kuti Satana angapezere mpata pa ife, pajatu timadziwa machenjerero ake.

Atumiki a Pangano Latsopano

12 Tsono nditafika ku Trowa kuti ndilalikire Uthenga Wabwino wa Khristu, nʼkupeza kuti Ambuye anditsekulira khomo, 13 ndinasowa mtendere mu mtima mwanga, chifukwa sindinapezeko mʼbale wanga Tito. Choncho ndinatsanzikana ndi anthu kumeneko nʼkupita ku Makedoniya.

14 Koma tithokoze Mulungu amene amatitsogolera nthawi zonse monga ogwidwa ku nkhondo a Khristu pa chipambano chake. Tsono amatigwiritsa ntchito yofalitsa ponseponse nzeru zodziwira Khristu ngati fungo labwino. 15 Pakuti kwa Mulungu ndife fungo labwino la Khristu pakati pa iwo amene akupulumutsidwa ndi amene akuwonongeka. 16 Kwa amene akuwonongeka ndife fungo la imfa, limawapha. Ndipo kwa amene akupulumuka ndife fungo lamoyo, limawapatsa moyo. Ndani angayithe ntchito yotereyi? 17 Kusiyana ndi ena ambiri, ife sitilalikira Mawu a Mulungu kuti tipeza phindu. Mʼmalo mwake, ife mwa Khristu timayankhula pamaso pa Mulungu moona mtima, monga anthu otumidwa ndi Mulungu.