Add parallel Print Page Options

基督照圣经所记的复活了

15 弟兄们,我要把我从前传给你们的福音向你们讲明。这福音你们已经领受了,并且靠着它站立得稳。 你们若持守我所传给你们的道,就必靠这福音得救,不然就是徒然相信了。 我从前领受了又传交给你们那最要紧的,就是基督照着圣经所记的,为我们的罪死了, 又埋葬了,又照着圣经所记的,第三天复活了; 并且曾经向矶法显现,然后向十二使徒显现。 以后又有一次向五百多个弟兄显现。他们中间大多数到现今还在,也有些已经睡了。 以后也向雅各显现,再后又向众使徒显现, 最后也向我显现;我好象一个未到产期而生的人。 我原是使徒中最小的,本来没有资格称为使徒,因为我曾经迫害 神的教会。 10 然而靠着 神的恩典,我得以有了今天,而且他赐给我的恩典并没有落空;我比众使徒格外劳苦,其实不是我,而是 神的恩典与我同在。 11 因此,不论是我,或是众使徒,我们这样传,你们也这样信了。

死人都要复活

12 我们既然传基督从死人中复活了,你们中间怎么有人说没有死人复活呢? 13 倘若没有死人复活的事,基督也就没有复活了。 14 如果基督没有复活,我们所传的就是枉然,你们的信也是枉然, 15 我们也会被人认为是替 神作假见证的了,因为我们为 神作过见证说,他使基督复活了。如果死人没有复活, 神也就没有使基督复活了。 16 因为如果死人没有复活,基督也就没有复活。 17 基督若没有复活,你们的信就是徒然,你们仍在你们的罪里。 18 那么,在基督里睡了的人也就灭亡了。 19 如果我们在基督里只在今生有盼望,就比所有人更可怜了。

20 现在基督已经从死人中复活,成为睡了的人初熟的果子。 21 死既借着一人而来,死人复活也借着一人而来。 22 在亚当里众人都死了,照样,在基督里众人也都要复活; 23 只是各人要按着自己的次序:初熟的果子是基督,以后,在他来的时候,是那些属基督的人。 24 再后,末期到了的时候,基督把所有的统治者、掌权者和有能者都毁灭了,就把国度交给父 神。 25 因为基督必要作王,直到 神把所有的仇敌都放在他的脚下。 26 最后要毁灭的仇敌就是死, 27 因为经上记着说:“他使万物都服在他脚下。”既然说万物都服了他,显然那使万物服他的就不包括在内了。 28 等到万物都服了他,那时子自己也要服那位叫万物服他的,好使 神在万有之上。

29 不然,那些为死人受洗的,是为了甚么呢?如果死人根本不会复活,那么为甚么要为他们受洗呢? 30 我们又为甚么时刻冒险呢? 31 弟兄们,我是天天冒死的,这是我凭着我在我们的主耶稣基督里,因你们而夸口说的。 32 我在以弗所和野兽搏斗,如果照着人的意思来看,那对我有甚么益处呢?如果死人不会复活,

“我们就吃吃喝喝吧,

因为我们明天就要死了。”

33 你们不要自欺,

“滥交朋友是会败坏品德的。”

34 你们理当醒悟过来,不要犯罪,因为你们中间有人不认识 神;我说这话是要你们羞愧。

复活的身体

35 但有人会说:“死人怎样复活呢?要带着怎么样的身体来呢?” 36 无知的人哪,你所种的若不死去,就不能生。 37 你们所种的,不是那将来要长成的形体,只不过是一粒种子,也许是麦子或别的种子。 38 但 神随着自己的意思给它一个形体,给每一样种子各有自己的形体。 39 而且各种身体也都不一样,人有人的身体,兽有兽的身体,鸟有鸟的身体,鱼有鱼的身体。 40 有天上的形体,也有地上的形体;天上形体的荣光是一样,地上形体的荣光又是一样。 41 太阳有太阳的荣光,月亮有月亮的荣光,星星有星星的荣光,而且每一颗星的荣光也都不同。

42 死人复活也是这样。所种的是必朽坏的,复活的是不朽坏的; 43 所种的是卑贱的,复活的是荣耀的;所种的是软弱的,复活的是有能力的; 44 所种的是属血气的身体,复活的是属灵的身体。既然有属血气的身体,也会有属灵的身体。 45 经上也是这样记着说:“第一个人亚当成了有生命的活人,末后的亚当成了使人活的灵。” 46 但那首先的不是属灵的,而是属血气的,然后才有属灵的。 47 第一个人是出于地,是属土的;第二个人是出于天。 48 那属土的怎样,所有属土的也都怎样;属天的怎样,所有属天的也都怎样。 49 我们既然有了属土的形象,将来也必有属天的形象。

50 弟兄们,我告诉你们,血肉之体不能承受 神的国,必朽坏的也不能承受那不朽坏的。 51-52 我现在把一个奥秘告诉你们:我们不是都要睡觉,而是在一剎那,眨眼之间,就是号角最后一次吹响的时候,我们都要改变;因为号角要吹响,死人要复活,成为不朽坏的,我们也要改变。 53 这必朽坏的必须穿上不朽坏的,这必死的必须穿上不死的; 54 这必朽坏的既穿上了不朽坏的,这必死的既穿上了不死的,那时,经上的话就应验了:

“胜利了!死亡已经被吞灭。

55 死亡啊!你的胜利在哪里?

死亡啊!你的毒刺在哪里?”

56 死的毒刺就是罪,罪的权势就是律法。 57 感谢 神,他借着我们的主耶稣基督,把胜利赐给我们。 58 所以,我亲爱的弟兄们,你们务要坚固,不可动摇,常常竭力多作主工,因为知道你们的劳苦,在主里面不是徒然的。

Za Kuuka kwa Khristu

15 Tsono abale, ndikufuna ndikukumbutseni za Uthenga Wabwino umene ndinakulalikirani. Munawulandira ndipo munawukhulupirira kolimba. Inu munapulumutsidwa ndi Uthenga Wabwinowu, ngati mwasunga mawu amene ndinakulalikirani. Kupanda kutero, mwangokhulupirira pachabe.

Pakuti chimene ndinalandira ndinapereka kwa inu monga chofunika kuposa zonse, kuti Khristu anafera zoyipa zathu monga mwa Malemba, kuti anayikidwa mʼmanda, kuti anaukitsidwa tsiku lachitatu monga mwa Malemba; ndipo kuti anaonekera kwa Petro, ndipo kenaka kwa Atumwi khumi ndi awiriwo. Pambuyo pake, Iye anaonekera kwa anthu oposa 500 mwa abale pa nthawi imodzi, ndipo ambiri mwa iwo akanali ndi moyo ngakhale kuti ena anagona tulo. Kenaka anaonekeranso kwa Yakobo, kenaka kwa atumwi onse. Potsiriza pa onse anaonekeranso kwa ine, monga mwana wobadwa nthawi isanakwane.

Pakuti ine ndine wamngʼono kwa atumwi ndipo sindiyenera nʼkomwe kutchedwa mtumwi chifukwa ndinazunza mpingo wa Mulungu. 10 Koma mwachisomo cha Mulungu, ndili mmene ndililimu, ndipo chisomo chake kwa ine sichinali chopanda ntchito. Ndinagwira ntchito kuposa ena onse a iwo. Choncho sindine koma chisomo cha Mulungu chimene chinali ndi ine. 11 Tsono kaya ndi ineyo kapena iwowo, izi ndi zomwe timalalikira, ndipo izi ndi zimene munakhulupirira.

Kuuka kwa Oyera Mtima

12 Koma ngati timalalikira kuti Khristu anaukitsidwa kwa akufa, zikutheka bwanji kuti ena mwa inu azinena kuti kulibe kuuka kwa akufa? 13 Ngati kulibe kuuka kwa akufa, ndiye kuti ngakhale Khristu sanaukenso. 14 Ndipo ngati Khristu sanaukitsidwe, ndiye kuti kulalikira kwathu nʼkopanda ntchito, ndipo chikhulupiriro chanu nʼchopandanso ntchito. 15 Kuwonjezera pamenepa, ndiye kuti ndife mboni zabodza pa za Mulungu, pakuti tikuchita umboni kuti Mulungu anaukitsa Khristu kwa akufa. Ngati nʼzoona kuti akufa saukitsidwa, ndiye kuti Mulungu sanaukitsenso Khristu. 16 Pakuti ngati akufa saukitsidwa, ndiye kuti nayenso Khristu sanaukitsidwe. 17 Ndipo ngati Khristu sanaukitsidwe, chikhulupiriro chanu nʼchopanda ntchito; mukanali mu machimo anu. 18 Ndiye kuti nawonso amene agona tulo mwa Ambuye ndi otayika. 19 Ngati kukanakhala kuti tili ndi chiyembekezo mwa Khristu mʼmoyo uno wokha, tikanakhala omvetsa chisoni kuposa anthu ena onse.

20 Koma nʼzoonadi kuti Khristu anaukitsidwa kwa kufa, chipatso choyamba cha onse ogona tulo. 21 Pakuti monga imfa inadza kudzera mwa munthu, kuuka kwa akufa kwabweranso kudzera mwa munthu. 22 Pakuti monga mwa Adamu onse amafa, chomwechonso mwa Khristu onse adzakhala ndi amoyo. 23 Koma aliyense adzauka pa nthawi yake. Khristu ndiye woyambirira, pambuyo pake, pamene Khristu adzabwera, iwo amene ali ake adzauka. 24 Pamenepo chimaliziro chidzafika, pamene Iye adzapereka ufumu kwa Mulungu Atate, atathetsa ufumu wonse, ulamuliro wonse ndi mphamvu zonse. 25 Pakuti Iye ayenera kulamulira mpaka Mulungu atayika pansi pa mapazi ake adani ake onse. 26 Mdani wotsiriza kuwonongedwa ndi imfa. 27 Pakuti Mulungu “wayika zinthu zonse pansi pa mapazi ake.” Ponena kuti wayika “zinthu zonse pansi pa mapazi ake,” nʼchodziwikiratu kuti sakuphatikizapo ndi Mulungu yemwe, amene anayika zinthu zonse pansi pa Khristu. 28 Pamene adzatsiriza kuchita zimenezi, Mwana weniweniyo adzakhala pansi pa ulamuliro wa Iye amene anayika zinthu zonse pansi pake, kuti Mulungu akhale zonse mu zonse.

29 Tsono ngati kulibe kuuka kwa akufa, kodi iwo amene akubatizidwa chifukwa cha akufa, adzatani? Ngati akufa saukitsidwa nʼkomwe, bwanji nanga anthu akubatizidwa mʼmalo mwawo? 30 Ndipo kwa ife, tikuyikiranji moyo wathu pachiswe nthawi ndi nthawi? 31 Abale, ndimafa tsiku ndi tsiku, ndikunenetsa zimenezi, mongotsimikizira monga ndimakunyadirani mwa Khristu Yesu Ambuye athu. 32 Ngati ndinalimbana ndi zirombo za kuthengo ku Efeso pa zifukwa za umunthu chabe, ndapindulanji? Ngati akufa sadzaukitsidwa,

“Tiyeni tidye ndi kumwa,
    pakuti mawa tifa.”

33 Musasocheretsedwe, “Kukhala mʼmagulu oyipa kumawononga makhalidwe abwino.” 34 Ganizani bwino monga kuyenerera, ndiye lekani kuchimwa; pakuti pali ena amene sadziwa Mulungu. Ndikunena izi kuti muchite manyazi.

Kuukitsidwa kwa Thupi

35 Koma wina akhoza kufunsa kuti, “Kodi akufa amaukitsidwa motani? Adzauka ndi thupi la mtundu wanji?” 36 Wopusa iwe! Chimene mudzala sichikhala ndi moyo pokhapokha chitayamba chafa. 37 Mukadzala, simudzala thupi limene lidzamere, koma mbewu chabe, mwina ya tirigu kapena ya china chake. 38 Koma Mulungu amayipatsa thupi monga Iye wafunira, ku mbewu ya mtundu uliwonse amapereka thupi lakelake. 39 Mnofu siwofanana. Anthu ali ndi mnofu wa mtundu wina, nyama zili ndi wina, mbalame zili ndi wina, nsomba zili ndi winanso. 40 Palinso matupi akumwamba ndipo palinso matupi a dziko lapansi; koma ulemerero wa matupi akumwamba ndi wina, ndi wa matupi a dziko lapansi ndi winanso. 41 Dzuwa lili ndi ulemerero wake, ndipo pali ulemerero wina wa mwezi, palinso ulemerero winanso wa nyenyezi. Ulemerero wa nyenyezi ndi wosiyanasiyana.

42 Zidzaterenso pamene akufa adzauka. Thupi loyikidwa mʼnthaka ngati mbewu limavunda, koma likadzauka lidzakhala losavunda. 43 Limayikidwa mʼmanda mopanda ulemu, koma likadzaukitsidwa lidzakhala ndi ulemerero. Limayikidwa mʼmanda lili lofowoka, koma likadzaukitsidwa lidzakhala ndi mphamvu. 44 Limayikidwa mʼmanda thupi la mnofu chabe, koma likadzaukitsidwa lidzakhala lauzimu.

Ngati pali thupi la mnofu, palinso thupi lauzimu. 45 Kwalembedwa kuti, “Munthu woyamba Adamu anakhala wamoyo,” Adamu wotsiriza anakhala wopatsa moyo. 46 Zauzimu sizinabwere koyambirira, koma zachilengedwe, pambuyo pake zauzimu. 47 Munthu woyamba anali wa dziko lapansi, wochokera mʼnthaka koma munthu wachiwiri anali wochokera kumwamba. 48 Monga analili munthu wa dziko lapansi, momwemonso anthu onse amene ndi a dziko lapansi. Ndipo monga alili munthu wakumwamba, momwemonso anthu onse amene ndi akumwamba. 49 Ndipo monga momwe tinabadwa ofanana ndi munthu wa dziko lapansi uja, momwemonso tidzakhala ofanana ndi munthu wakumwamba.

50 Ndikunenetsa, abale, kuti thupi ndi magazi sizingathe kulowa mu ufumu wa Mulungu, ndipo zimene zimavunda sizingathe kulowa kumene zinthu sizivunda. 51 Tamverani, ndikuwuzeni chinsinsi. Tonse sitidzagona tulo, koma tonse tidzasandulika. 52 Zidzachitika mwadzidzidzi, mʼkamphindi kochepa, monga ngati kuphethira kwa diso, pa lipenga lotsiriza. Pakuti lipenga lidzalira, akufa adzaukitsidwa opanda chovunda, ndipo ife tidzasandulika. 53 Pakuti chovunda chiyenera kuvala chosavunda, ndi thupi ili lakufa liyenera kuvala losafa. 54 Pamene thupi lovundali likadzasanduka losavunda, ndipo thupi lotha kufali likadzasanduka losatha kufa, pamenepo zidzakwaniritsidwa zimene zinalembedwa zakuti, “Imfa yogonjetsedwa kwathunthu.”

55 “Iwe imfa, kupambana kwako kuli kuti?
    Iwe imfa, ululu wako uli kuti?”

56 Ululu wa imfa ndi tchimo, ndipo mphamvu ya tchimo ndi lamulo. 57 Koma tiyamike Mulungu amene amatipambanitsa mwa Ambuye athu Yesu Khristu.

58 Choncho, abale anga okondedwa imani njii. Musasunthike ndi chilichonse. Nthawi zonse mudzipereke kwathunthu ku ntchito ya Ambuye, chifukwa mukudziwa kuti ntchito zanu mwa Ambuye sizili zopanda phindu.