Add parallel Print Page Options
'歷 代 志 下 34 ' not found for the version: Chinese New Testament: Easy-to-Read Version.

犹大王约西亚

34 约西亚八岁登基,在耶路撒冷执政三十一年。 他做耶和华视为正的事,效法他祖先大卫,不偏不离。

约西亚清除偶像

他执政第八年,虽然还年幼,却开始寻求他祖先大卫的上帝。他执政第十二年,开始清除犹大和耶路撒冷的丘坛、亚舍拉神像、雕刻和铸造的偶像。 众人在他面前拆毁巴力的祭坛,他砍掉高高的香坛,又把亚舍拉神像及雕刻和铸造的偶像磨成粉末,撒在祭拜它们之人的坟墓上, 把它们祭司的骸骨放在它们的坛上焚烧。这样,他洁净了犹大和耶路撒冷。 约西亚还在玛拿西、以法莲、西缅,远至拿弗他利的各城邑及其周围的荒废之地做了同样的事情。 他拆毁祭坛和亚舍拉神像,把偶像磨成粉末,砍掉以色列境内所有的香坛,然后回到耶路撒冷。

发现律法书

约西亚执政第十八年,洁净国土和圣殿以后,就差遣亚萨利雅的儿子沙番、耶路撒冷的总督玛西雅和约哈斯的儿子约亚史官负责整修他的上帝耶和华的殿。 他们到希勒迦大祭司那里,把献给上帝殿的银子交给他。这银子是守殿门的利未人从玛拿西人和以法莲人,所有剩下的以色列人,所有的犹大人和便雅悯人,以及耶路撒冷的居民那里收来的。 10 他们把银子交给负责管理耶和华殿的督工,由他们转交给整修耶和华殿的工人, 11 也就是木匠和石匠,让他们用来购买凿好的石头、木架和栋梁,整修犹大诸王毁坏的殿。 12 工人都忠诚地工作。他们的督工是利未人米拉利的子孙雅哈和俄巴底,哥辖的子孙撒迦利亚和米书兰。其他精通乐器的利未人 13 负责监督搬运工人,还有一些做书记、官员和殿门守卫。

14 他们把奉献到耶和华殿里的银子拿出来的时候,希勒迦祭司发现了摩西所传的耶和华的律法书。 15 希勒迦就对沙番书记说:“我在耶和华的殿里发现了律法书。”希勒迦就把书卷交给沙番。 16 沙番把书卷带到王那里,向王禀告说:“凡交给仆人们办的事,都已办妥。 17 耶和华殿里的银子已被取出来交给督工和工人。” 18 沙番书记又对王说:“希勒迦祭司交给我一卷书。”沙番就在王面前诵读这书。 19 王听了律法书上的话,就撕裂衣服, 20 吩咐希勒迦、沙番的儿子亚希甘、米迦的儿子亚比顿、沙番书记和王的臣仆亚撒雅: 21 “你们去为我、为以色列和犹大的余民求问耶和华有关这书卷上的话。耶和华的烈怒已经临到我们身上,因为我们的祖先没有遵守耶和华的话,没有遵行这书卷上的话。”

22 于是,王派去的人跟着希勒迦去求问女先知户勒妲,她是负责管理礼服的沙龙之妻。沙龙是哈斯拉的孙子、特瓦的儿子。户勒妲住在耶路撒冷第二区。他们向她说明来意, 23 她对他们说:“以色列的上帝耶和华要你们回去告诉差你们来见我的人, 24 耶和华说,‘我要照在犹大王面前所读的那书上的一切咒诅,降灾难给这地方及这里的居民。 25 因为他们背弃我,给别的神明烧香,制造偶像惹我发怒,所以我的怒火要在这地方燃烧,绝不止息。’ 26 你们告诉差你们来求问耶和华的犹大王,‘至于你所听见的那些话,以色列的上帝耶和华说, 27 因为你听到我对这地方及这里居民的警告,便悔改,在我面前谦卑、撕裂衣服,向我哭泣,我垂听了你的祷告。这是我耶和华说的。 28 我会让你平安入土,你不会看到我要降给这地方及这里居民的一切灾难。’”他们便回去禀告王。

约西亚立约顺服上帝

29 于是,王召集犹大和耶路撒冷的所有长老, 30 与犹大人和耶路撒冷的居民、祭司和利未人等全体民众,不论贵贱,一同上到耶和华的殿。王把在耶和华殿中发现的约书念给他们听。 31 王站在自己的位置上,在耶和华面前立约,要全心全意地跟随耶和华,遵从祂的一切诫命、法度和律例,履行约书上的规定。 32 他使耶路撒冷和便雅悯的人都遵行这约。于是,耶路撒冷的居民都遵行他们祖先的上帝的约。 33 约西亚除去以色列境内所有的可憎之物,又吩咐所有住在以色列的人都事奉他们的上帝耶和华。约西亚在世时,他们都没有偏离他们祖先的上帝耶和华。

Yosiya Akonzanso Chipembedzo

34 Yosiya anali wa zaka zisanu ndi zitatu pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu kwa zaka 31. Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova ndi kutsata makhalidwe a Davide abambo ake, osatembenukira kumanja kapena kumanzere.

Mʼchaka chachisanu ndi chitatu cha ulamuliro wake, iye akanalibe wamngʼono, anayamba kufunafuna Mulungu wa Davide abambo ake. Mʼchaka cha khumi ndi chiwiri iye anayamba kuyeretsa Yuda ndi Yerusalemu kuchotsa malo azipembedzo, mafano a Asera, milungu yosema ndi mafano owumbidwa. Maguwa ansembe a Baala anagwetsedwa iye atalamulira. Anadula zidutswazidutswa maguwa ofukizira lubani amene anali pamwamba pake, ndipo anaphwanya mafano a Asera, milungu ndi zifaniziro zake. Anaziperapera ndipo anaziwaza pamwamba pa manda a amene ankapereka nsembe kwa mafanowo. Iye anatentha mafupa a ansembe pa maguwa awo, kotero iye anayeretsa Yuda ndi Yerusalemu. Ku mizinda ya Manase, Efereimu ndi Simeoni mpaka kufika ku Nafutali, ndiponso malo a mabanja owazungulira, iye anagwetsa maguwa ansembe ndi mafano a Asera ndi kuphwanyaphwanya milungu yawo kukhala fumbi ndi kuduladula maguwa ofukizapo lubani mʼdziko lonse la Israeli. Atatero, anabwerera ku Yerusalemu.

Mʼchaka cha 18 cha ulamuliro wa Yosiya, atayeretsa dziko ndi Yerusalemu, Yosiya anatuma Safani mwana wa Azariya ndi Maaseya, wolamulira mzinda pamodzi ndi Yowa mwana wa Yowahazi mlembi wolemba mbiri, kuti akonze Nyumba ya Yehova Mulungu wake.

Iwo anapita kwa Hilikiya, mkulu wa ansembe ndipo anamupatsa ndalama zimene zinaperekedwa mʼNyumba ya Mulungu, zimene Alevi amene anali alonda apakhomo analandira kuchokera kwa anthu a ku Manase, Efereimu ndi onse otsala a ku Israeli ndiponso anthu onse ochokera ku Yuda ndi Benjamini ndi okhala mu Yerusalemu. 10 Ndipo anazipereka mʼmanja mwa anthu amene anasankhidwa kuti ayangʼanire ntchito ya Nyumba ya Yehova. Anthu amenewa ankalipira antchito amene ankakonzanso Nyumba ya Mulungu. 11 Iwo anaperekanso ndalama kwa amisiri a matabwa ndi amisiri omanga nyumba kuti agule miyala yosema ndi matabwa a phaso la nyumba ndi nsichi zomangira zomwe mfumu ya Yuda inalekerera kuti zigwe ndi kuwonongeka.

12 Anthuwa anagwira ntchitoyi mokhulupirika. Amene ankawayangʼanira anali Yahati ndi Obadiya, Alevi ochokera ku banja la Merari, ndi Zekariya ndi Mesulamu ochokera ku banja la Kohati. Alevi onse amene anali aluso loyimbira zida za nyimbo 13 ankayangʼanira anthu onyamula katundu, namatsogolera anthu onse amene ankagwira ntchito iliyonse yotumikira. Alevi ena anali alembi, akapitawo ndiponso alonda apamakomo.

Buku la Malamulo Lipezeka

14 Pa nthawi imene ankatulutsa ndalama zimene anabwera nazo ku Nyumba ya Yehova, wansembe Hilikiya anapeza Buku la Malamulo limene linaperekedwa kudzera mwa Mose. 15 Hilikiya anati kwa Safani, mlembi wa zochitika, “Ine ndapeza Buku la Malamulo mʼNyumba ya Yehova.” Iye analipereka kwa Safani.

16 Ndipo Safani anapita nalo bukulo kwa mfumu ndi kumufotokozera kuti: “Akuluakulu anu akuchita zonse zimene zinapatsidwa kwa iwo. 17 Iwo alipira ndalama zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndipo azipereka kwa akapitawo ndi anthu antchito.” 18 Kenaka Safani, mlembi wa zochitika anawuza mfumu, “Wansembe, Hilikiya wandipatsa ine buku ili.” Ndipo Safani anawerenga bukulo pamaso pa mfumu.

19 Mfumu itamva mawu a Buku la Malamulo, inangʼamba mkanjo wake. 20 Iye analamula izi kwa Hilikiya, Ahikamu mwana wa Safani, Abidoni mwana wa Mika, Safani mlembi wa zochitika ndi Asaya mtumiki wa mfumu: 21 “Pitani ndipo mukafunse Yehova mʼmalo mwanga ndi mʼmalo mwa otsala a Israeli ndi Yuda za zimene zalembedwa mʼbuku limene lapezekali. Mkwiyo wa Yehova ndi waukulu umene watsanulidwa pa ife chifukwa makolo athu sanasunge mawu a Yehova. Iwo sanachite motsatira zonse zimene zalembedwa mʼbuku ili.”

22 Hilikiya pamodzi ndi anthu amene anawatuma aja, anapita kukayankhula ndi mneneri wamkazi Hulida, amene anali mkazi wa Salumu mwana wa Tokati, mwana wa Hasira, wosunga zovala zaufumu. Hulida ankakhala mu Yerusalemu, mʼdera lachiwiri la mzindawo.

23 Iye anati kwa anthuwo, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, muwuzeni munthu amene wakutumani kwa ineyo kuti, 24 ‘Yehova akunena kuti, Ine ndidzabweretsa mavuto pamalo pano ndi pa anthu ake, matemberero onse amene alembedwa mʼbukuli amene awerengedwa pamaso pa mfumu ya Yuda. 25 Chifukwa iwo anasiya Ine ndi kufukiza lubani kwa milungu ina ndi kuwutsa mkwiyo wanga ndi zonse zimene manja awo anapanga, mkwiyo wanga udzatsanulidwa pamalo pano ndipo sudzazimitsidwa.’ 26 Uzani mfumu ya Yuda imene yakutumani kuti mudzafunse kwa Yehova Mulungu wa Israeli, ‘Chimene Yehova, Mulungu wa Israeli akunena mokhudzana ndi mawu amene mwamva ndi ichi: 27 Pakuti mtima wako walapa, ndipo wadzichepetsa wekha pamaso pa Mulungu pamene unamva zimene Iye ananena motsutsa malo ano ndi anthu ake, ndipo chifukwa iwe unadzichepetsa wekha pamaso pa Ine ndi kungʼamba zovala zako ndi kulira pamaso panga, ndamva pemphero lako, atero Yehova. 28 Tsono Ine ndidzakutengera kwa makolo ako, ndipo udzayikidwa mʼmanda mwamtendere. Maso ako sadzaona mavuto onse amene Ine ndidzabweretsa pa malo ano ndi pa iwo amene amakhala pano.’ ”

Choncho iwo anatenga yankho lakelo ndi kubwerera kwa mfumu.

29 Ndipo mfumu inasonkhanitsa pamodzi akuluakulu onse a Yuda ndi Yerusalemu. 30 Iye anapita ku Nyumba ya Yehova pamodzi ndi anthu a Yuda, anthu a mu Yerusalemu, ansembe ndi Alevi, anthu onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu. Iye anawerenga pamaso pawo mawu onse a Buku la Chipangano, limene linapezeka mʼNyumba ya Yehova. 31 Mfumu inayimirira pa chipilala chake ndipo inachitanso pangano pamaso pa Yehova: kutsatira Yehova, ndi kusunga malamulo ake, machitidwe ake ndi malangizo ake ndi mtima wake wonse ndi moyo wake wonse, ndi kumvera mawu a pangano olembedwa mʼbukulo.

32 Tsono Yosiya anawuza aliyense amene anali mu Yerusalemu ndi Benjamini kuti azisunga panganoli. Anthu a mu Yerusalemu anachita izi motsata pangano la Mulungu, Mulungu wa makolo awo.

33 Yosiya anachotsa mafano onse onyansa mʼdziko lonse limene linali la Aisraeli ndipo anawuza onse amene anali mu Israeli kutumikira Yehova Mulungu wawo. Pa masiku onse a moyo wake, iye sanaleke kutsatira Yehova, Mulungu wa makolo awo.