使徒行传 23
Chinese New Version (Simplified)
23 保罗定睛看着公议会的各人,说:“各位弟兄,我在 神面前,行事为人一向都是凭着良心的。” 2 大祭司亚拿尼亚就吩咐站在他旁边的人打保罗的嘴巴。 3 保罗对他说:“你这粉饰的墙啊, 神要击打你!你坐堂要按着律法审问我,现在你竟然违背律法吩咐人打我吗?” 4 站在旁边的人民说:“你敢辱骂 神的大祭司吗?” 5 保罗说:“弟兄们,我不知道他是大祭司。经上说:‘不可咒诅你人民的领袖。’”
6 保罗看出其中一部分是撒都该人,另一部分是法利赛人,就在公议会中大声说:“我是法利赛人,也是法利赛人的子孙,我现在受审,是为了盼望死人复活!” 7 他说了这话,法利赛人和撒都该人就起了争论,会众也分裂了,成为两派。 8 原来撒都该人说没有复活,没有天使,也没有鬼灵,法利赛人却认定这些都有。 9 于是众人大嚷大闹,有几个法利赛派的经学家站起来辩论说:“我们看不出这个人作过甚么坏事;说不定有灵或天使对他说过话。” 10 争论越来越大,千夫长怕保罗被他们撕碎了,就吩咐士兵下去,把他从人群中抢救出来,带到营楼去。
11 当天晚上,主站在保罗身边,说:“你要壮起胆来,你怎样在耶路撒冷作见证,也必照样在罗马为我作见证。”
犹太人设计谋害保罗
12 到了天亮,犹太人在一起秘密计谋,并且发誓说,不杀保罗,就不吃不喝。 13 一同策划这项阴谋的有四十多人。 14 他们来见众祭司长和长老,说:“我们已经发了誓,不杀保罗,就不吃东西。 15 现在你们和公议会要通知千夫长,带保罗到你们这里来,装作要详细审查他。我们已经预备好了,不等他走近,就把他杀了。” 16 但保罗的外甥听见这项埋伏的诡计,就到营楼去,告诉保罗。 17 保罗请了一个百夫长来,说:“请你带这个青年人去见千夫长,他有事要报告。” 18 百夫长就带保罗的外甥去见千夫长,说:“囚犯保罗请了我去,求我带这个青年人来见你,他有事要向你报告。” 19 千夫长拉着他的手,走到一边,私下问他:“你有甚么事要向我报告?” 20 他说:“犹太人已经约好了,要求你明天把保罗带到公议会里去,装作要详细审查他。 21 你不要听他们,因为他们有四十多人正在埋伏起来等着保罗;他们发了誓,不杀保罗,就不吃不喝。现在他们已经准备好了,只等你答应。” 22 千夫长嘱咐那青年人:“不要告诉人你把这事告诉了我。”然后就打发他走了。
保罗被交送腓力斯
23 千夫长叫了两个百夫长来,说:“预备两百个步兵,七十个骑兵、两百个长枪手,晚上九点钟往该撒利亚去。 24 也要预备好牲口,好让保罗骑上,护送他安全到达腓力斯总督那里。” 25 千夫长写了一封信,大意如下:
26 “革老丢.吕西亚问候总督腓力斯大人。 27 这个人被犹太人捉住,快要遭害的时候,我听说他是罗马公民,就带兵去把他救出来。 28 为要知道犹太人控告他的原因,我就带他到他们的公议会那里去。 29 我发现他被控告,是为了他们律法上的问题,并没有甚么该死该绑的罪名。 30 后来我接到密报,得知害他的阴谋,就立刻把他送到你那里去,并且吩咐原告到你面前来控告他。”
31 于是士兵照着吩咐,把保罗提出来,连夜带到安提帕底。 32 第二天,他们把保罗交给骑兵队护送,就回营楼去了。 33 骑兵到了该撒利亚,把信呈上总督,同时把保罗也交给他。 34 总督读了信,就问保罗是哪一省的人;知道了他是基利家人, 35 就说:“等到原告也来了,我才审问你。”于是吩咐人把他拘留在希律的王府里。
Machitidwe a Atumwi 23
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
23 Paulo anayangʼanitsitsa anthu a Bwalo Lalikulu nati, “Abale anga, ndakhala ndi chikumbumtima chabwino pamaso pa Mulungu mpaka lero lino.” 2 Chifukwa cha mawu amenewa, mkulu wa ansembe Ananiya analamulira amene anali pafupi ndi Paulo kuti amumenye pakamwa. 3 Pamenepo Paulo anamuwuza kuti, “Mulungu adzakukantha, iwe munthu wachiphamaso! Wakhala pamenepo kuti undiweruze ine monga mwalamulo, koma iweyo ukuphwanya lamulolo polamulira kuti andimenye!”
4 Anthu amene anayimirira pafupi ndi Paulo anati, “Bwanji ukunyoza mkulu wa ansembe wa Mulungu?”
5 Paulo anayankha nati, “Abale, ine sindinazindikire kuti ndi mkulu wa ansembe; pakuti kunalembedwa kuti, ‘Usayankhule zoyipa kwa mtsogoleri wa anthu ako.’ ”
6 Paulo atazindikira kuti ena mwa iwo anali Asaduki ndiponso ena anali Afarisi, anafuwula mʼbwalo muja kuti, “Abale anga, ine ndine Mfarisi, mwana wa Mfarisi. Ndikuweruzidwa chifukwa cha chiyembekezo cha kuuka kwa akufa.” 7 Iye atanena zimenezi, mkangano unabuka pakati pa Afarisi ndi Asaduki mpaka anthu kugawikana. 8 Asaduki amati kulibe kuuka kwa akufa, kulibenso ngakhale angelo kapena mizimu, koma Afarisi amakhulupirira zonsezi.
9 Panali phokoso lalikulu, ndipo aphunzitsi ena amalamulo amene anali a gulu la Afarisi anayimirira natsutsa kwambiri. Iwo anati, “Ife sitikupeza cholakwa ndi munthu uyu, chifukwa mwina ndi mzimu kapena mngelo amene wayankhula naye.” 10 Mkangano unakula kwambiri kotero kuti mkulu wa asilikali anachita mantha kuti mwina anthu angakhadzule Paulo. Iye analamulira asilikali ake apite kukamuchotsa pakati pawo mwamphamvu ndi kubwera naye ku malo a asilikaliwo.
11 Usiku omwewo Ambuye anayimirira pambali pa Paulo nati, “Limba mtima! Monga wandichitira Ine umboni mu Yerusalemu, moteronso uyenera kundichitira umboni ku Roma.”
Ayuda Achita Chiwembu Paulo
12 Kutacha Ayuda ena anakonza chiwembu ndipo analumbira kuti sadya kapena kumwa mpaka atapha Paulo. 13 Anthu amene anakonza chiwembuchi analipo makumi anayi. 14 Iwo anapita kwa akulu a ansembe ndi akuluakulu a Ayuda nakawawuza kuti, “Ife talumbira kolimba kuti sitidya kalikonse mpaka titapha Paulo. 15 Tsopano inu pamodzi ndi akuluakulu a Bwalo Lalikulu mupemphe mkulu wa asilikali kuti akubweretsereni Paulo ngati kuti mukufuna kudziwa bwino za mlandu wake. Ife takonzeka kudzamupha asanafike kumeneko.”
16 Koma mwana wa mlongo wake wa Paulo atamva za chiwembuchi, anapita ku malo a asilikali aja namufotokozera Paulo.
17 Paulo anayitana mmodzi wa wolamulira asilikali 100 aja, namuwuza kuti, “Pita naye mnyamatayu kwa mkulu wa asilikali. Iyeyu ali ndi mawu oti akamuwuze.” 18 Anamutengadi mnyamatayo napita naye kwa mkulu wa asilikali uja, nati, “Wamʼndende uja Paulo anandiyitana, nandipempha kuti ndibweretse mnyamatayu kwa inu chifukwa ali ndi kanthu koti akuwuzeni.”
19 Mkulu wa asilikali uja anagwira dzanja mnyamatayo napita naye paseli ndipo anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna kuti undiwuze chiyani?”
20 Mnyamatayo anati, “Ayuda agwirizana zoti akupempheni kuti mawa mubwere ndi Paulo ku Bwalo Lalikulu, ngati kuti akufuna kudziwa bwino za iye. 21 Inu musawamvere, chifukwa pali anthu opitirira makumi anayi amene akumudikirira pa njira. Iwo alumbira kuti sadya kapena kumwa mpaka atapha Paulo. Panopa ndi okonzeka kale, akungodikira kuti muwavomere pempho lawo.”
22 Mkulu wa asilikaliyo anawuza mnyamatayo kuti apite koma anamuchenjeza kuti, “Usawuze munthu aliyense kuti wandifotokozera zimenezi.”
Paulo Apita ku Kaisareya
23 Kenaka mkulu wa asilikaliyo anayitana awiri a asilikali olamulira asilikali 100 nawalamula kuti, “Uzani asilikali 200, asilikali 70 okwera pa akavalo ndi 200 onyamula mikondo kuti akonzeke kupita ku Kaisareya usiku omwe uno nthawi ya 9 koloko. 24 Mumukonzerenso Paulo akavalo woti akwerepo kuti akafike bwino kwa bwanamkubwa Felike.”
25 Iye analemba kalata iyi:
26 Ine Klaudiyo Lusiya,
Kwa wolemekezeka, bwanamkubwa Felike:
Ndikupereka moni.
27 Munthuyo Ayuda anamugwira ndipo anali pafupi kumupha, koma ine ndinapita ndi asilikali nʼkukamulanditsa pakuti ndinamva kuti ndi nzika ya Chiroma. 28 Ndinkafuna kudziwa mlandu umene anapalamula, choncho ndinapita naye ku Bwalo lawo Lalikulu. 29 Ine ndinapeza kuti amamuyimba mlandu wa nkhani ya malamulo awo, koma panalibe mlandu woyenera kumuphera kapena kumuyika mʼndende. 30 Nditawuzidwa kuti amukonzera chiwembu munthuyu, ine ndamutumiza kwa inu msanga. Ine ndalamulanso amene akumuyimba mlanduwo kuti abwere kwa inu kudzafotokoza nkhaniyo.
31 Pamenepo asilikali aja anatenga Paulo monga anawalamulira napita naye ku Antipatri usiku. 32 Mmawa mwake iwo anabwerera ku malo a asilikali nasiya okwera pa akavalo kuti apitirire ndi Paulo. 33 Asilikali okwera pa akavalowo atafika ku Kaisareya anapereka kalatayo kwa bwanamkubwa, namuperekanso Paulo. 34 Bwanamkubwayo anawerenga kalatayo ndipo anamufunsa Paulo za dera limene amachokera. Atazindikira kuti amachokera ku Kilikiya, 35 iye anati, “Ndidzamva mlandu wako okuyimba mlandu akabwera kuno.” Ndipo analamulira kuti asilikali adzimulondera Paulo ku nyumba ya mfumu Herode.
Chinese New Version (CNV). Copyright © 1976, 1992, 1999, 2001, 2005 by Worldwide Bible Society.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.