Add parallel Print Page Options

Mawu a Zofari

20 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti

“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe
    chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
Ndikumva kudzudzula kondinyoza,
    ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.

“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale,
    kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha,
    chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba
    ndipo mutu wake uli nengʼaa,
iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe;
    iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso,
    adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
Diso limene linamuona silidzamuonanso;
    sadzapezekanso pamalo pake.
10 Ana ake adzabwezera zonse
    zimene iyeyo analanda anthu osauka;
11 Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake
    zidzagona naye limodzi mʼfumbi.

12 “Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake
    ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
13 ngakhale salola kuzilavula,
    ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
14 koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake;
    chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
15 Adzachisanza chuma chimene anachimeza;
    Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
16 Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo
    ululu wa mphiri udzamupha.
17 Sadzasangalala ndi timitsinje,
    mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
18 Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya;
    sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
19 Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo;
    iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.

20 “Chifukwa choti umbombo wake sutha,
    sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
21 Palibe chatsala kuti iye adye;
    chuma chake sichidzachedwa kutha.
22 Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera;
    mavuto aakulu adzamugwera.
23 Akadya nʼkukhuta,
    Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto
    ngati mvula yosalekeza.
24 Ngakhale athawe mkondo wachitsulo,
    muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
25 Muviwo adzawutulutsira ku msana,
    songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake.
Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
26     mdima wandiweyani ukudikira chuma chake.
Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza
    ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
27 Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake;
    dziko lapansi lidzamuwukira.
28 Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake,
    katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
29 Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa,
    mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”

Zophar

20 Then Zophar the Naamathite(A) replied:

“My troubled thoughts prompt me to answer
    because I am greatly disturbed.(B)
I hear a rebuke(C) that dishonors me,
    and my understanding inspires me to reply.

“Surely you know how it has been from of old,(D)
    ever since mankind[a] was placed on the earth,
that the mirth of the wicked(E) is brief,
    the joy of the godless(F) lasts but a moment.(G)
Though the pride(H) of the godless person reaches to the heavens(I)
    and his head touches the clouds,(J)
he will perish forever,(K) like his own dung;
    those who have seen him will say, ‘Where is he?’(L)
Like a dream(M) he flies away,(N) no more to be found,
    banished(O) like a vision of the night.(P)
The eye that saw him will not see him again;
    his place will look on him no more.(Q)
10 His children(R) must make amends to the poor;
    his own hands must give back his wealth.(S)
11 The youthful vigor(T) that fills his bones(U)
    will lie with him in the dust.(V)

12 “Though evil(W) is sweet in his mouth
    and he hides it under his tongue,(X)
13 though he cannot bear to let it go
    and lets it linger in his mouth,(Y)
14 yet his food will turn sour in his stomach;(Z)
    it will become the venom of serpents(AA) within him.
15 He will spit out the riches(AB) he swallowed;
    God will make his stomach vomit(AC) them up.
16 He will suck the poison(AD) of serpents;
    the fangs of an adder will kill him.(AE)
17 He will not enjoy the streams,
    the rivers(AF) flowing with honey(AG) and cream.(AH)
18 What he toiled for he must give back uneaten;(AI)
    he will not enjoy the profit from his trading.(AJ)
19 For he has oppressed the poor(AK) and left them destitute;(AL)
    he has seized houses(AM) he did not build.

20 “Surely he will have no respite from his craving;(AN)
    he cannot save himself by his treasure.(AO)
21 Nothing is left for him to devour;
    his prosperity will not endure.(AP)
22 In the midst of his plenty, distress will overtake him;(AQ)
    the full force of misery will come upon him.(AR)
23 When he has filled his belly,(AS)
    God will vent his burning anger(AT) against him
    and rain down his blows on him.(AU)
24 Though he flees(AV) from an iron weapon,
    a bronze-tipped arrow pierces him.(AW)
25 He pulls it out of his back,
    the gleaming point out of his liver.
Terrors(AX) will come over him;(AY)
26     total darkness(AZ) lies in wait for his treasures.
A fire(BA) unfanned will consume him(BB)
    and devour what is left in his tent.(BC)
27 The heavens will expose his guilt;
    the earth will rise up against him.(BD)
28 A flood will carry off his house,(BE)
    rushing waters[b] on the day of God’s wrath.(BF)
29 Such is the fate God allots the wicked,
    the heritage appointed for them by God.”(BG)

Footnotes

  1. Job 20:4 Or Adam
  2. Job 20:28 Or The possessions in his house will be carried off, / washed away