Add parallel Print Page Options

Atsogoleri ndi Aneneri Adzudzulidwa

Ndipo ine ndinati,

“Tamverani, inu atsogoleri a Yakobo,
    inu olamulira nyumba ya Israeli.
Kodi sindinu oyenera kudziwa kuweruza molungama,
    inu amene mumadana ndi zabwino ndi kukonda zoyipa;
inu amene mumasenda khungu la anthu anga,
    ndipo mumakungunula mnofu pa mafupa awo;
inu amene mumadya anthu anga,
    mumasenda khungu lawo
    ndi kuphwanya mafupa awo;
inu amene mumawadula nthulinthuli
    ngati nyama yokaphika?”

Pamenepo adzalira kwa Yehova,
    koma Iye sadzawayankha.
Nthawi imeneyo Iye adzawabisira nkhope yake
    chifukwa cha zoyipa zimene anazichita.

Yehova akuti,

“Aneneri amene
    amasocheretsa anthu anga,
ngati munthu wina awapatsa chakudya
    amamufunira ‘mtendere;’
ngati munthu wina sawapatsa zakudya
    amamulosera zoyipa.
Nʼchifukwa chake kudzakuderani,
    simudzaonanso masomphenya,
mdima udzakugwerani ndipo simudzawombezanso.
    Dzuwa lidzawalowera aneneriwo, ndipo mdima udzawagwera.
Alosi adzachita manyazi
    ndipo owombeza mawula adzanyazitsidwa.
Onse adzaphimba nkhope zawo
    chifukwa Mulungu sakuwayankha.”

Koma kunena za ine, ndadzazidwa ndi mphamvu,
    ndi Mzimu wa Yehova,
    ndi kulungama, ndi kulimba mtima,
kuti ndilalikire za kugalukira kwa Yakobo,
    kwa Israeli za tchimo lake.
Imvani izi, inu atsogoleri a nyumba ya Yakobo,
    inu olamulira nyumba ya Israeli,
inu amene mumadana ndi kuweruza kolungama;
    ndipo mumakhotetsa zinthu zonse zolondola;
10 inu amene mukumanga Ziyoni pokhetsa magazi,
    ndi Yerusalemu ndi kuyipa kwanu.
11 Atsogoleri ake amalandira chiphuphu kuti aweruze,
    ansembe ake amalandira malipiro kuti alalikire,
    ndipo aneneri ake amanenera kuti alandire ndalama.
Komatu amatsamira pa Yehova nʼkumanena kuti,
    “Kodi Yehova sali pakati pathu?
    Palibe tsoka limene lidzatigwere.”
12 Choncho chifukwa cha inu,
    Ziyoni adzatipulidwa ngati munda,
Yerusalemu adzasanduka bwinja,
    ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.

Leaders and Prophets Rebuked

Then I said,

“Listen, you leaders(A) of Jacob,
    you rulers of Israel.
Should you not embrace justice,
    you who hate good and love evil;
who tear the skin from my people
    and the flesh from their bones;(B)
who eat my people’s flesh,(C)
    strip off their skin
    and break their bones in pieces;(D)
who chop(E) them up like meat for the pan,
    like flesh for the pot?(F)

Then they will cry out to the Lord,
    but he will not answer them.(G)
At that time he will hide his face(H) from them
    because of the evil they have done.(I)

This is what the Lord says:

“As for the prophets
    who lead my people astray,(J)
they proclaim ‘peace’(K)
    if they have something to eat,
but prepare to wage war against anyone
    who refuses to feed them.
Therefore night will come over you, without visions,
    and darkness, without divination.(L)
The sun will set for the prophets,(M)
    and the day will go dark for them.(N)
The seers will be ashamed(O)
    and the diviners disgraced.(P)
They will all cover(Q) their faces(R)
    because there is no answer from God.(S)
But as for me, I am filled with power,
    with the Spirit of the Lord,
    and with justice and might,
to declare to Jacob his transgression,
    to Israel his sin.(T)

Hear this, you leaders of Jacob,
    you rulers of Israel,
who despise justice
    and distort all that is right;(U)
10 who build(V) Zion with bloodshed,(W)
    and Jerusalem with wickedness.(X)
11 Her leaders judge for a bribe,(Y)
    her priests teach for a price,(Z)
    and her prophets tell fortunes for money.(AA)
Yet they look(AB) for the Lord’s support and say,
    “Is not the Lord among us?
    No disaster will come upon us.”(AC)
12 Therefore because of you,
    Zion will be plowed like a field,
Jerusalem will become a heap of rubble,(AD)
    the temple(AE) hill a mound overgrown with thickets.(AF)