Add parallel Print Page Options

135 Tamandani Yehova.

Tamandani dzina la Yehova;
    mutamandeni, inu atumiki a Yehova,
amene mumatumikira mʼnyumba ya Yehova,
    mʼmabwalo a nyumba ya Mulungu wathu.

Tamandani Yehova, pakuti Yehova ndi wabwino;
    imbani nyimbo zotamanda dzina lake, pakuti nʼkokoma kutero,
Pakuti Yehova wasankha Yakobo kuti akhale wake,
    Israeli kuti akhale chuma chake chapamtima.

Ndikudziwa kuti Yehova ndi wamkulu,
    kuti Ambuye athu ndi wamkulu kuposa milungu yonse.
Yehova amachita chilichonse chimene chimamukomera,
    kumwamba ndi dziko lapansi,
    ku nyanja zazikulu ndi ku malo ake onse akuya.
Iye amatulutsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi,
    amatumiza zingʼaningʼani pamodzi ndi mvula
    ndipo amatulutsa mphepo ku malo ake osungiramo.

Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto,
    ana oyamba kubadwa a anthu ndi nyama.
Iye anatumiza zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa pakati pako, iwe Igupto,
    kutsutsana ndi Farao pamodzi ndi atumiki ake onse.
10 Iye anakantha mitundu yambiri ya anthu
    ndi kupha mafumu amphamvu:
11 Sihoni mfumu ya Aamori,
    Ogi mfumu ya Basani,
    ndi maufumu onse a ku Kanaani;
12 ndipo anapereka dziko lawo ngati cholowa,
    cholowa cha anthu ake Aisraeli.

13 Dzina lanu, Inu Yehova, ndi losatha mpaka muyaya,
    mbiri yanu, Inu Yehova, idziwika mibado yonse.
14 Pakuti Yehova adzaonetsa kuti anthu ake ngosalakwa,
    ndipo adzachitira chifundo atumiki ake.

15 Mafano a mitundu ya anthu ndi siliva ndi golide,
    opangidwa ndi manja a anthu.
16 Pakamwa ali napo koma sayankhula
    maso ali nawo, koma sapenya;
17 makutu ali nawo, koma sakumva
    ndipo mʼkamwa mwawo mulibe mpweya uliwonse.
18 Iwo amene amapanga mafanowo adzakhala ngati mafanowo,
    chimodzimodzinso iwo amene amadalira mafanowo.

19 Inu nyumba ya Israeli, tamandani Yehova;
    inu nyumba ya Aaroni, tamandani Yehova;
20 Inu nyumba ya Levi, tamandani Yehova;
    Inu amene mumaopa Iye, tamandani Yehova.
21 Wodalitsika ndi Yehova kuchokera mʼZiyoni,
    amene amakhala mu Yerusalemu.

Tamandani Yehova.

Psalm 135(A)

Praise the Lord.[a]

Praise the name of the Lord;
    praise him, you servants(B) of the Lord,
you who minister in the house(C) of the Lord,
    in the courts(D) of the house of our God.

Praise the Lord, for the Lord is good;(E)
    sing praise to his name,(F) for that is pleasant.(G)
For the Lord has chosen Jacob(H) to be his own,
    Israel to be his treasured possession.(I)

I know that the Lord is great,(J)
    that our Lord is greater than all gods.(K)
The Lord does whatever pleases him,(L)
    in the heavens and on the earth,(M)
    in the seas and all their depths.
He makes clouds rise from the ends of the earth;
    he sends lightning with the rain(N)
    and brings out the wind(O) from his storehouses.(P)

He struck down the firstborn(Q) of Egypt,
    the firstborn of people and animals.
He sent his signs(R) and wonders into your midst, Egypt,
    against Pharaoh and all his servants.(S)
10 He struck down many(T) nations
    and killed mighty kings—
11 Sihon(U) king of the Amorites,(V)
    Og king of Bashan,(W)
    and all the kings of Canaan(X)
12 and he gave their land as an inheritance,(Y)
    an inheritance to his people Israel.

13 Your name, Lord, endures forever,(Z)
    your renown,(AA) Lord, through all generations.
14 For the Lord will vindicate his people(AB)
    and have compassion on his servants.(AC)

15 The idols of the nations(AD) are silver and gold,
    made by human hands.(AE)
16 They have mouths, but cannot speak,(AF)
    eyes, but cannot see.
17 They have ears, but cannot hear,
    nor is there breath(AG) in their mouths.
18 Those who make them will be like them,
    and so will all who trust in them.

19 All you Israelites, praise the Lord;(AH)
    house of Aaron, praise the Lord;
20 house of Levi, praise the Lord;
    you who fear him, praise the Lord.
21 Praise be to the Lord from Zion,(AI)
    to him who dwells in Jerusalem.(AJ)

Praise the Lord.

Footnotes

  1. Psalm 135:1 Hebrew Hallelu Yah; also in verses 3 and 21