Add parallel Print Page Options

Israeli Akolola Kamvuluvulu

“Ika lipenga pakamwa pako.
    Ngati chiwombankhanga, kutsutsana ndi nyumba ya Yehova
chifukwa anthu aphwanya pangano langa
    ndiponso agalukira lamulo langa.
Israeli akulirira kwa Ine kuti,
    ‘Inu Mulungu wathu, ife timakudziwani!’
Koma Israeli wakana zabwino;
    mdani adzamuthamangitsa.
Amalonga mafumu mosatsata kufuna kwanga.
    Amasankha akalonga popanda chilolezo changa.
Amadzipangira mafano
    asiliva ndi agolide
    koma adzawonongeka nawo.
Iwe Samariya, taya fano lako la mwana wangʼombe!
    Mkwiyo wanga wayakira anthuwo.
Padzapita nthawi yayitali chotani asanasinthike kukhala oyera mtima?
    Mafanowa ndi ochokera ku Israeli!
Mwana wa ngʼombe uyu anapangidwa ndi munthu waluso;
    si Mulungu amene anamupanga.
Adzaphwanyidwa nʼkukhala zidutswa,
    mwana wangʼombe wa ku Samariya.

“Aisraeli amadzala mphepo
    ndipo amakolola kamvuluvulu.
Tirigu alibe ngala;
    sadzabala chakudya.
Akanabala chakudya
    alendo akanadya chakudyacho.
Israeli wamezedwa,
    tsopano ali pakati pa anthu a mitundu ina
    ngati chinthu cha chabechabe.
Pakuti iwo anapita ku Asiriya
    ngati mbidzi yongodziyendera pa yokha.
    Efereimu wadzigulitsa kwa zibwenzi zake.
10 Ngakhale wadzigulitsa pakati pa mitundu ya anthu,
    Ine ndidzawasonkhanitsa pamodzi.
Iwo adzayamba kuzunzika pansi pa
    ulamuliro wankhanza wa mfumu yamphamvu.

11 “Ngakhale Efereimu anamanga maguwa ambiri a nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo,
    maguwa amenewa akhala malo ochimwirapo.
12 Ndinawalembera zinthu zambiri za malamulo anga,
    koma iwo anaziyesa ngati zinthu zachilendo.
13 Amapereka nsembe za nyama kwa Ine
    ndipo iwo amadya nyamayo,
    koma Yehova sakondwera nazo.
Tsopano Iye adzakumbukira zoyipa zawo
    ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo:
    iwowo adzabwerera ku Igupto.
14 Israeli wayiwala Mlengi wake
    ndipo wamanga nyumba zaufumu;
    Yuda wachulukitsa mizinda ya malinga.
Koma Ine ndidzaponya moto pa mizinda yawoyo,
    moto umene udzatenthe malinga awo.”

Israel to Reap the Whirlwind

“Put the trumpet(A) to your lips!
    An eagle(B) is over the house of the Lord
because the people have broken my covenant(C)
    and rebelled against my law.(D)
Israel cries out to me,
    ‘Our God, we acknowledge you!’
But Israel has rejected what is good;
    an enemy will pursue him.(E)
They set up kings without my consent;
    they choose princes without my approval.(F)
With their silver and gold
    they make idols(G) for themselves
    to their own destruction.
Samaria, throw out your calf-idol!(H)
    My anger burns against them.
How long will they be incapable of purity?(I)
    They are from Israel!
This calf—a metalworker has made it;
    it is not God.(J)
It will be broken in pieces,
    that calf(K) of Samaria.(L)

“They sow the wind
    and reap the whirlwind.(M)
The stalk has no head;
    it will produce no flour.(N)
Were it to yield grain,
    foreigners would swallow it up.(O)
Israel is swallowed up;(P)
    now she is among the nations
    like something no one wants.(Q)
For they have gone up to Assyria(R)
    like a wild donkey(S) wandering alone.
    Ephraim has sold herself to lovers.(T)
10 Although they have sold themselves among the nations,
    I will now gather them together.(U)
They will begin to waste away(V)
    under the oppression of the mighty king.

11 “Though Ephraim built many altars for sin offerings,
    these have become altars for sinning.(W)
12 I wrote for them the many things of my law,
    but they regarded them as something foreign.(X)
13 Though they offer sacrifices as gifts to me,
    and though they eat(Y) the meat,
    the Lord is not pleased with them.(Z)
Now he will remember(AA) their wickedness
    and punish their sins:(AB)
    They will return to Egypt.(AC)
14 Israel has forgotten(AD) their Maker(AE)
    and built palaces;
    Judah has fortified many towns.
But I will send fire on their cities
    that will consume their fortresses.”(AF)