Hoseya 8
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Israeli Akolola Kamvuluvulu
8 “Ika lipenga pakamwa pako.
Ngati chiwombankhanga, kutsutsana ndi nyumba ya Yehova
chifukwa anthu aphwanya pangano langa
ndiponso agalukira lamulo langa.
2 Israeli akulirira kwa Ine kuti,
‘Inu Mulungu wathu, ife timakudziwani!’
3 Koma Israeli wakana zabwino;
mdani adzamuthamangitsa.
4 Amalonga mafumu mosatsata kufuna kwanga.
Amasankha akalonga popanda chilolezo changa.
Amadzipangira mafano
asiliva ndi agolide
koma adzawonongeka nawo.
5 Iwe Samariya, taya fano lako la mwana wangʼombe!
Mkwiyo wanga wayakira anthuwo.
Padzapita nthawi yayitali chotani asanasinthike kukhala oyera mtima?
6 Mafanowa ndi ochokera ku Israeli!
Mwana wa ngʼombe uyu anapangidwa ndi munthu waluso;
si Mulungu amene anamupanga.
Adzaphwanyidwa nʼkukhala zidutswa,
mwana wangʼombe wa ku Samariya.
7 “Aisraeli amadzala mphepo
ndipo amakolola kamvuluvulu.
Tirigu alibe ngala;
sadzabala chakudya.
Akanabala chakudya
alendo akanadya chakudyacho.
8 Israeli wamezedwa,
tsopano ali pakati pa anthu a mitundu ina
ngati chinthu cha chabechabe.
9 Pakuti iwo anapita ku Asiriya
ngati mbidzi yongodziyendera pa yokha.
Efereimu wadzigulitsa kwa zibwenzi zake.
10 Ngakhale wadzigulitsa pakati pa mitundu ya anthu,
Ine ndidzawasonkhanitsa pamodzi.
Iwo adzayamba kuzunzika pansi pa
ulamuliro wankhanza wa mfumu yamphamvu.
11 “Ngakhale Efereimu anamanga maguwa ambiri a nsembe zoperekedwa chifukwa cha tchimo,
maguwa amenewa akhala malo ochimwirapo.
12 Ndinawalembera zinthu zambiri za malamulo anga,
koma iwo anaziyesa ngati zinthu zachilendo.
13 Amapereka nsembe za nyama kwa Ine
ndipo iwo amadya nyamayo,
koma Yehova sakondwera nazo.
Tsopano Iye adzakumbukira zoyipa zawo
ndi kuwalanga chifukwa cha machimo awo:
iwowo adzabwerera ku Igupto.
14 Israeli wayiwala Mlengi wake
ndipo wamanga nyumba zaufumu;
Yuda wachulukitsa mizinda ya malinga.
Koma Ine ndidzaponya moto pa mizinda yawoyo,
moto umene udzatenthe malinga awo.”
Hosea 8
New International Version
Israel to Reap the Whirlwind
8 “Put the trumpet(A) to your lips!
An eagle(B) is over the house of the Lord
because the people have broken my covenant(C)
and rebelled against my law.(D)
2 Israel cries out to me,
‘Our God, we acknowledge you!’
3 But Israel has rejected what is good;
an enemy will pursue him.(E)
4 They set up kings without my consent;
they choose princes without my approval.(F)
With their silver and gold
they make idols(G) for themselves
to their own destruction.
5 Samaria, throw out your calf-idol!(H)
My anger burns against them.
How long will they be incapable of purity?(I)
6 They are from Israel!
This calf—a metalworker has made it;
it is not God.(J)
It will be broken in pieces,
that calf(K) of Samaria.(L)
7 “They sow the wind
and reap the whirlwind.(M)
The stalk has no head;
it will produce no flour.(N)
Were it to yield grain,
foreigners would swallow it up.(O)
8 Israel is swallowed up;(P)
now she is among the nations
like something no one wants.(Q)
9 For they have gone up to Assyria(R)
like a wild donkey(S) wandering alone.
Ephraim has sold herself to lovers.(T)
10 Although they have sold themselves among the nations,
I will now gather them together.(U)
They will begin to waste away(V)
under the oppression of the mighty king.
11 “Though Ephraim built many altars for sin offerings,
these have become altars for sinning.(W)
12 I wrote for them the many things of my law,
but they regarded them as something foreign.(X)
13 Though they offer sacrifices as gifts to me,
and though they eat(Y) the meat,
the Lord is not pleased with them.(Z)
Now he will remember(AA) their wickedness
and punish their sins:(AB)
They will return to Egypt.(AC)
14 Israel has forgotten(AD) their Maker(AE)
and built palaces;
Judah has fortified many towns.
But I will send fire on their cities
that will consume their fortresses.”(AF)
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.