Masalimo 123
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu.
123 Ndikweza maso anga kwa Inu,
kwa Inu amene mumakhala kumwamba.
2 Taonani, monga momwe maso a akapolo amayangʼana mʼdzanja la mbuye wawo,
monga momwenso maso a mdzakazi amayangʼana mʼdzanja la dona wake,
choncho maso athu ali kwa Yehova Mulungu wathu,
mpaka atichitire chifundo.
3 Mutichitire chifundo, Inu Yehova mutichitire chifundo,
pakuti tapirira chitonzo chachikulu.
4 Ife tapirira mnyozo wambiri kuchokera kwa anthu odzikuza,
chitonzo chachikulu kuchokera kwa anthu onyada.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.