Add parallel Print Page Options

Mayina a Mafumu Ogonjetsedwa

12 Aisraeli anagonjetsa dziko lonse la kummawa kwa Yorodani, kuyambira ku chigwa cha Arinoni mpaka ku phiri la Herimoni pamodzi ndi dera lonse la kummawa kwa Araba. Iwo anatenga dzikoli kukhala lawo, ndipo mafumu a dzikoli anali awa:

Sihoni mfumu ya Aamori,

amene ankakhala mu Hesiboni. Iye analamulira kuyambira ku Aroeri mzinda umene uli mʼmphepete mwa mtsinje wa Arinoni, mpaka ku mtsinje wa Yaboki, umene uli mʼmalire mwa Aamori, kuphatikizanso theka la dziko la Giliyadi. Iye ankalamuliranso dera la chigwa cha Yorodani kuyambira ku Nyanja ya Kinereti, kummawa ndi kumatsika mpaka ku Beti-Yesimoti, mzinda umene unali kummawa kwa Nyanja ya Mchere ndi kutsikabe kummwera mpaka pa tsinde pa phiri la Pisiga.

Ogi mfumu ya mzinda wa Basani,

amene anali mmodzi mwa otsala mwa Arefaimu. Iye ankakhala ku Asiteroti ndi Ederi. Dera la ufumu wake linafika ku phiri la Herimoni, ku Saleka ndi dziko lonse la Basani mpaka ku malire ndi anthu a ku Gesuri Makati. Ufumu wake unaphatikizanso theka la Giliyadi mpaka ku malire a mfumu Sihoni ya ku Hesiboni.

Mose mtumiki wa Yehova ndi Aisraeli anawagonjetsa ndipo anapereka dziko lawo kwa anthu a fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti chikhale cholowa chawo.

Yoswa ndi Aisraeli onse anagonjetsa mafumu onse okhala kumadzulo kwa mtsinje wa Yorodani kuyambira ku Baala-Gadi, ku chigwa cha Lebanoni mpaka ku phiri la Halaki, kumapita cha ku Seiri. Yoswa anagawira dzikolo mafuko a Israeli kuti likhale cholowa chawo. Dziko limeneli linali dera la ku mapiri, chigwa cha kumadzulo, chigwa cha Yorodani, ku matsitso a kummawa, ndi dziko la chipululu la kummwera. Amene ankakhala mʼdzikoli anali Ahiti, Aamori, Akanaani, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi. Mafumu ake anali awa:

mfumu ya Yerikoimodzi
mfumu ya Ai (kufupi ndi Beteliimodzi
10 mfumu ya Yerusalemuimodzi
mfumu ya Hebroniimodzi
11 mfumu ya Yarimutiimodzi
mfumu ya Lakisiimodzi
12 mfumu ya Egiloniimodzi
mfumu ya Gezeriimodzi
13 mfumu ya Debriimodzi
mfumu ya Gederiimodzi
14 mfumu ya Horimaimodzi
mfumu ya Aradiimodzi
15 mfumu ya Libinaimodzi
mfumu ya Adulamuimodzi
16 mfumu ya Makedaimodzi
mfumu ya Beteliimodzi
17 mfumu ya Tapuwaimodzi
mfumu ya Heferiimodzi
18 mfumu ya Afekiimodzi
mfumu ya Lasaroniimodzi
19 mfumu ya Madoniimodzi
mfumu ya Hazoriimodzi
20 mfumu ya Simuroni Meroniimodzi
mfumu ya Akisafuimodzi
21 mfumu ya Taanakiimodzi
mfumu ya Megidoimodzi
22 mfumu ya Kadesiimodzi
mfumu ya Yokineamu ku Karimeliimodzi
23 mfumu ya Dori ku Nafoti Doriimodzi
mfumu ya Goyini ku Giligalaimodzi
24 mfumu ya Tirizaimodzi
mafumu onse pamodzi analipo 31.