Add parallel Print Page Options

Za Kulangidwa kwa Kusi

18 Tsoka kwa anthu a ku Kusi.
    Kumeneko kumamveka mkokomo wa mapiko a dzombe.
Dziko limenelo limatumiza akazembe pa mtsinje wa Nailo,
    mʼmabwato amabango amene amayandama pa madzi,
ndikunena kuti, “Pitani, inu amithenga aliwiro,
kwa mtundu wa anthu ataliatali a khungu losalala,
    ndi woopedwa ndi anthu.
Akazembe anatumidwa ku dziko la anthu amphamvu ndi logonjetsa anthu ena.
    Dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.”

Inu nonse anthu a pa dziko lonse,
    inu amene mumakhala pa dziko lapansi,
pamene mbendera yakwezedwa pa mapiri
    yangʼanani,
ndipo pamene lipenga lilira
    mumvere.
Pakuti Yehova akunena kwa ine kuti,
    “Ndili chikhalire ku malo anga kuno, ndidzakhala chete, ndi kumangoyangʼana,
monga momwe dzuwa limawalira nthawi yotentha,
    monganso momwe mame amagwera usiku pa nthawi yotentha yokolola.”
Pakuti, anthu asanayambe kukolola, maluwa atayoyoka
    ndiponso mphesa zitayamba kupsa,
Iye adzadula mphukira ndi mipeni yosadzira,
    ndipo adzadula ndi kuchotsa nthambi zotambalala.
Mitembo ya anthu ankhondo adzasiyira mbalame zamʼmapiri zodya nyama
    ndiponso zirombo zakuthengo;
mbalame zidzadya mitemboyo nthawi yonse ya chilimwe,
    ndipo zirombo zidzayidya pa nthawi yonse yachisanu.

Pa nthawi imeneyo anthu adzabwera ndi mphatso kwa Yehova Wamphamvuzonse,

zochokera kwa anthu ataliatali ndi osalala,
    kuchokera kwa mtundu wa anthu woopedwa ndi anthu apafupi ndi akutali omwe,
mtundu wa anthu amphamvu ndi a chiyankhulo chachilendo,
    anthu amene dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.

Adzabwera nazo mphatso ku Phiri la Ziyoni, ku malo a Dzina la Yehova Wamphamvuzonse.