Add parallel Print Page Options

Nyimbo. Salimo la Asafu.

83 Inu Mulungu musakhale chete;
    musangoti phee, Mulungu musangoti duu.
Onani adani anu akuchita chiwawa,
    amene amadana nanu autsa mitu yawo.
Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu;
    Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.
Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu
    kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”

Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu;
    Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:
Matenti a Edomu ndi Aismaeli,
    Mowabu ndi Ahagiri,
Agebala, Aamoni ndi Aamaleki,
    Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.
Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo
    kupereka mphamvu kwa ana a Loti.
            Sela

Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani,
    monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.
10 Amene anawonongedwa ku Endori
    ndi kukhala ngati zinyalala.
11 Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu
    ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,
12 amene anati, “Tiyeni tilande dziko
    la msipu la Mulungu.”

13 Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga,
    ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.
14 Monga moto umatentha nkhalango,
    kapena malawi a moto kuyatsa phiri,
15 kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho,
    ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.
16 Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi
    kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.

17 Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse;
    awonongeke mwa manyazi.
18 Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova,
    ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.