Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Salimo la Asafu.

80 Tcherani khutu Inu mʼbusa wa Israeli,
    Inu amene mumatsogolera Yosefe monga nkhosa;
Inu amene mumakhala pa mpando waufumu pakati pa akerubi, walani
    kwa Efereimu, Benjamini ndi Manase.
Utsani mphamvu yanu;
    bwerani ndi kutipulumutsa.

Tibwezereni mwakale Inu Mulungu;
    nkhope yanu itiwalire
    kuti tipulumutsidwe.

Inu Mulungu Wamphamvuzonse,
    mpaka liti mkwiyo wanu udzanyeka
    kutsutsana ndi mapemphero a anthu anu?
Mwawadyetsa buledi wa misozi;
    mwachitisa iwo kumwa misozi yodzaza mbale.
Mwachititsa kuti tikhale gwero la mikangano pakati pa anansi athu,
    ndipo adani athu akutinyoza.

Tibwezereni mwakale Inu Mulungu Wamphamvuzonse,
    nkhope yanu itiwalire
    kuti tipulumutsidwe.

Munatulutsa mpesa kuchoka ku Igupto;
    munathamangitsa anthu a mitundu ina ndi kuwudzala mpesawo.
Munawulimira munda wamphesawo,
    ndipo unamera ndi kudzaza dziko.
10 Mapiri anaphimbidwa ndi mthunzi wake,
    mikungudza yamphamvu ndi nthambi zake.
11 Unatambalitsa nthambi zake mpaka ku nyanja,
    mphukira zake mpaka ku mtsinje.

12 Chifukwa chiyani mwagwetsa makoma ake
    kuti onse amene akudutsa athyole mphesa zake?
13 Nguluwe zochokera mʼnkhalango zikuwononga
    ndipo zirombo za mthengo zimawudya.
14 Bweraninso kwa ife Inu Mulungu Wamphamvuzonse!
    Yangʼanani pansi muli kumwambako ndipo muone!
Uyangʼanireni mpesa umenewu,
15     muzu umene dzanja lanu lamanja ladzala,
    mwana amene inu munamukuza nokha.

16 Mpesa wanu wadulidwa ndi kutenthedwa ndi moto;
    pakudzudzula kwanu anthu anu awonongeka.
17 Dzanja lanu likhale pa munthu amene ali ku dzanja lanu lamanja,
    mwana wa munthu amene mwalera nokha.
18 Ndipo ife sitidzatembenukira kumbali kuchoka kwa Inu;
    titsitsimutseni ndipo tidzayitana pa dzina lanu.

19 Tibwezereni mwakale Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse
    nkhope yanu itiwalire
    kuti tipulumutsidwe.