Add parallel Print Page Options

Salimo la Davide.

103 Tamanda Yehova, iwe moyo wanga;
    ndi zonse zamʼkati mwanga zitamande dzina lake loyera.
Tamanda Yehova, iwe moyo wanga,
    ndipo usayiwale zabwino zake zonse.
Amene amakhululuka machimo ako onse
    ndi kuchiritsa nthenda zako zonse,
amene awombola moyo wako ku dzenje
    ndi kukuveka chikondi ndi chifundo chake ngati chipewa chaufumu,
amene akwaniritsa zokhumba zako ndi zinthu zabwino,
    kotero kuti umakhala wamphamvu zatsopano ngati mphungu.

Yehova amachita chilungamo
    ndipo amaweruza molungama onse opsinjika.

Iye anadziwitsa Mose njira zake,
    ntchito zake kwa Aisraeli.
Yehova ndi wachifundo ndi wokoma mtima,
    wosakwiya msanga ndi wachikondi chochuluka.
Iye sadzatsutsa nthawi zonse,
    kapena kusunga mkwiyo wake kwamuyaya;
10 satichitira molingana ndi machimo athu,
    kapena kutibwezera molingana ndi mphulupulu zathu.
11 Pakuti monga kumwamba kuli kutali ndi dziko lapansi,
    koteronso chikondi chake nʼchachikulu kwa iwo amene amamuopa;
12 monga kummawa kutalikirana ndi kumadzulo,
    koteronso Iye watichotsera mphulupulu zathu kuti zikhale kutali nafe.
13 Monga bambo amachitira chifundo ana ake,
    choncho Yehova ali ndi chifundo ndi iwo amene amamuopa;
14 pakuti Iye amadziwa momwe tinawumbidwira,
    amakumbukira kuti ndife fumbi.
15 Kunena za munthu, masiku ake ali ngati udzu,
    amaphuka ngati duwa la mʼmunda;
16 koma mphepo imawombapo ndipo silionekanso
    ndipo malo ake sakumbukirikanso.
17 Koma kuchokera muyaya mpaka muyaya
    chikondi cha Yehova chili ndi iwo amene amamuopa,
    ndi chilungamo chake chili ndi ana a ana awo;
18 iwo amene amasunga pangano lake
    ndi kukumbukira kumvera malangizo ake.

19 Yehova wakhazikitsa mpando wake waufumu mmwamba
    ndipo ufumu wake umalamulira onse.

20 Tamandani Yehova, inu angelo ake,
    amphamvu inu amene mumachita zimene amalamula,
    amene mumamvera mawu ake.
21 Tamandani Yehova, zolengedwa zonse zakumwamba,
    inu atumiki ake amene mumachita chifuniro chake.
22 Tamandani Yehova, ntchito yake yonse
    kulikonse mu ulamuliro wake.

Tamanda Yehova, iwe moyo wanga.