Add parallel Print Page Options

Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni
    ndi mtambo wa mkwiyo wake!
Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli
    kuchoka kumwamba.
Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso
    popondapo mapazi ake.

Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo;
mu mkwiyo wake anagwetsa
    malinga a mwana wamkazi wa Yuda.
Anagwetsa pansi mochititsa manyazi
    maufumu ndi akalonga ake.

Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola
    nyanga iliyonse ya Israeli.
Anabweza dzanja lake lamanja
    pamene mdani anamuyandikira.
Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa
    umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.

Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani;
    wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani,
ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira.
Ukali wake ukuyaka ngati moto
    pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.

Ambuye ali ngati mdani;
    wawonongeratu Israeli;
wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu
    ndipo wawononga malinga ake.
Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira
    kwa mwana wamkazi wa Yuda.

Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda;
    wawononga malo ake a msonkhano.
Yehova wayiwalitsa Ziyoni
    maphwando ake oyikika ndi masabata ake.
Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza
    mfumu ndi wansembe.

Ambuye wakana guwa lake la nsembe
    ndipo wasiya malo ake opatulika.
Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu
    kwa mdani wake;
adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova
    ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.

Yehova anatsimikiza kugwetsa
    makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni.
Anawayesa ndi chingwe
    ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa.
Analiritsa malinga ndi makoma;
    onse anawonongeka pamodzi.

Zipata za Yerusalemu zalowa pansi;
    wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake.
Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu,
    palibenso lamulo,
ndipo aneneri ake sakupeza
    masomphenya kuchokera kwa Yehova.

10 Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni
    akhala chete pansi;
awaza fumbi pa mitu yawo
    ndipo avala ziguduli.
Anamwali a Yerusalemu
    aweramitsa mitu yawo pansi.

11 Maso anga atopa ndi kulira,
    ndazunzika mʼmoyo mwanga,
mtima wanga wadzaza ndi chisoni
    chifukwa anthu anga akuwonongeka,
chifukwa ana ndi makanda akukomoka
    mʼmisewu ya mu mzinda.

12 Anawo akufunsa amayi awo kuti,
    “Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?”
pamene akukomoka ngati anthu olasidwa
    mʼmisewu ya mʼmizinda,
pamene miyoyo yawo ikufowoka
    mʼmanja mwa amayi awo.

13 Ndinganene chiyani za iwe?
    Ndingakufanizire ndi chiyani,
    iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu?
Kodi ndingakufanizire ndi yani
    kuti ndikutonthoze,
    iwe namwali wa Ziyoni?
Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja,
    kodi ndani angakuchiritse?

14 Masomphenya a aneneri ako
    anali abodza ndi achabechabe.
Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo
    poyika poyera mphulupulu zako.
Mauthenga amene anakupatsa
    anali achabechabe ndi osocheretsa.

15 Onse oyenda mʼnjira yako
    akukuwombera mʼmanja;
akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola
    iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu:
“Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa
    wokongola kotheratu,
    chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”

16 Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza;
iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo,
    ndipo akuti, “Tamumeza.
Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera;
    tili ndi moyo kuti tilione.”

17 Yehova wachita chimene anakonzeratu;
    wakwaniritsa mawu ake,
    amene anatsimikiza kale lomwe.
Wakuwononga mopanda chifundo,
    walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako,
    wakweza mphamvu za adani ako.

18 Mitima ya anthu
    ikufuwulira Ambuye.
Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni,
    misozi yako itsike ngati mtsinje
    usana ndi usiku;
usadzipatse wekha mpumulo,
    maso ako asaleke kukhetsa misozi.

19 Dzuka, fuwula usiku,
    pamene alonda ayamba kulondera;
khuthula mtima wako ngati madzi
    pamaso pa Ambuye.
Kweza manja ako kwa Iye
    chifukwa cha miyoyo ya ana ako,
amene akukomoka ndi njala
    mʼmisewu yonse ya mu mzinda.

20 Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani:
    kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi?
Kodi amayi adye ana awo,
    amene amawasamalira?
Kodi ansembe ndi aneneri awaphere
    mʼmalo opatulika a Ambuye?

21 Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi
    pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda;
anyamata anga ndi anamwali anga
    aphedwa ndi lupanga.
Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu;
    mwawapha mopanda chifundo.

22 Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando,
    chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse.
Pa tsiku limene Yehova wakwiya
    palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo;
mdani wanga wawononga
    onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.